< Jeremiah 47 >

1 The word of YHWH that came to Jeremiah the prophet concerning the Philistines, before that Pharaoh struck Gaza.
Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:
2 "Thus says YHWH: 'Look, waters rise up out of the north, and shall become an overflowing stream, and shall overflow the land and all that is in it, the city and those who dwell in it; and the men shall cry, and all the inhabitants of the land shall wail.
Yehova akuti, “Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto; adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo. Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo, mizinda ndi onse okhala mʼmenemo. Anthu adzafuwula; anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
3 At the noise of the stamping of the hoofs of his strong ones, at the rushing of his chariots, at the rumbling of his wheels, the fathers do not look back to their children for feebleness of hands;
akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga, phokoso la magaleta ake ndi kulira kwa mikombero yake. Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo; manja awo adzangoti khoba.
4 because of the day that comes to destroy all the Philistines, to cut off from Tyre and Sidon every helper who remains: for YHWH will destroy the Philistines, the remnant of the isle of Caphtor.
Pakuti tsiku lafika lowononga Afilisti onse ndi kupha onse otsala, onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni. Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti, otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
5 Baldness has come on Gaza; Ashkelon is brought to nothing, the remnant of their valley: how long will you cut yourself?
Anthu a ku Gaza ameta mipala; anthu a ku Asikeloni akhala chete. Inu otsala a ku chigwa, mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?
6 You sword of YHWH, "how long will it be before you be quiet? Put up yourself into your sheath; rest, and be still."
“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova, kodi udzapumula liti? Bwerera mʼmalo ako; ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
7 How can it be quiet, since YHWH has given you a command? Against Ashkelon, and against the seashore, there has he appointed it.'"
Koma lupangalo lidzapumula bwanji pamene Yehova walilamulira kuti lithire nkhondo Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”

< Jeremiah 47 >