< Jeremiah 35 >

1 The word which came to Jeremiah from YHWH in the days of Jehoiakim the son of Josiah, king of Judah, saying,
Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti:
2 "Go to the house of the Rechabites, and speak to them, and bring them into the house of YHWH, into one of the rooms, and give them wine to drink."
“Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”
3 Then I took Jaazaniah the son of Jeremiah, the son of Habazziniah, and his brothers, and all his sons, and the whole house of the Rechabites.
Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu.
4 And I brought them into the house of YHWH, into the room of the sons of Hananiah son of Gedaliah, the man of God, which was by the room of the officials, which was above the room of Maaseiah the son of Shallum, the keeper of the threshold.
Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo.
5 I set before the sons of the house of the Rechabites bowls full of wine, and cups; and I said to them, "Drink wine."
Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”
6 But they said, "We will drink no wine; for Jonadab the son of Rechab, our father, commanded us, saying, 'You shall drink no wine, neither you, nor your sons, forever:
Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale.
7 neither shall you build house, nor sow seed, nor plant vineyard, nor have any; but all your days you shall dwell in tents; that you may live many days in the land in which you live.'
Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’
8 We have obeyed the voice of Jonadab the son of Rechab, our father, in all that he commanded us, to drink no wine all our days, we, our wives, our sons, or our daughters;
Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo
9 nor to build houses for us to dwell in; neither have we vineyard, nor field, nor seed:
kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu.
10 but we have lived in tents, and have obeyed, and done according to all that Jonadab our father commanded us.
Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula.
11 But it happened, when Nebuchadnezzar king of Babylon came up into the land, that we said, 'Come, and let us go to Jerusalem for fear of the army of the Chaldeans, and for fear of the army of the Arameans'; so we dwell at Jerusalem."
Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”
12 Then came the word of YHWH to Jeremiah, saying,
Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti,
13 "Thus says YHWH of hosts, the God of Israel: 'Go, and tell the men of Judah and the inhabitants of Jerusalem, "Will you not receive instruction to listen to my words?" says YHWH.
“Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova.
14 "The words of Jonadab the son of Rechab, that he commanded his sons, not to drink wine, are performed; and to this day they drink none, for they obey their father's commandment: but I have spoken to you, rising up early and speaking; and you have not listened to me.
‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine.
15 I have sent also to you all my servants the prophets, rising up early and sending them, saying, 'Return now every man from his evil way, and amend your doings, and do not go after other gods to serve them, and you shall dwell in the land which I have given to you and to your fathers': but you have not inclined your ear, nor listened to me.
Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine.
16 Because the sons of Jonadab the son of Rechab have performed the commandment of their father which he commanded them, but this people has not listened to me;
Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.
17 therefore thus says YHWH, the God of hosts, the God of Israel: 'Look, I will bring on Judah and on all the inhabitants of Jerusalem all the disaster that I have pronounced against them; because I have spoken to them, but they have not listened; and I have called to them, but they have not answered.'"'"
“Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’”
18 Jeremiah said to the house of the Rechabites, "Thus says YHWH of hosts, the God of Israel: 'Because you have obeyed the commandment of Jonadab your father, and kept all his precepts, and done according to all that he commanded you';
Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.”
19 therefore thus says YHWH of hosts, the God of Israel: 'Jonadab the son of Rechab shall not want a man to stand before me forever.'"
Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”

< Jeremiah 35 >