< Jeremiah 26 >

1 In the beginning of the reign of Jehoiakim the son of Josiah, king of Judah, came this word from YHWH, saying,
Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 "Thus says YHWH: Stand in the court of YHWH's house, and speak to all the cities of Judah, which come to worship in YHWH's house, all the words that I command you to speak to them; do not diminish a word.
“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
3 It may be they will listen, and turn every man from his evil way; that I may relent of the evil which I purpose to do to them because of the evil of their doings.
Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
4 You shall tell them, 'Thus says YHWH: If you will not listen to me, to walk in my law, which I have set before you,
Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
5 to listen to the words of my servants the prophets, whom I send to you, even rising up early and sending them, but you have not listened;
ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
6 then will I make this house like Shiloh, and will make this city a curse to all the nations of the earth.'"
ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
7 The priests and the prophets and all the people heard Jeremiah speaking these words in the house of YHWH.
Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
8 It happened, when Jeremiah had made an end of speaking all that YHWH had commanded him to speak to all the people, that the priests and the prophets and all the people laid hold on him, saying, "You shall surely die.
Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
9 Why have you prophesied in the name of YHWH, saying, 'This house shall be like Shiloh, and this city shall be desolate, without inhabitant?'" All the people were gathered to Jeremiah in the house of YHWH.
Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
10 When the officials of Judah heard these things, they came up from the king's house to the house of YHWH; and they sat in the entry of the New Gate of YHWH's house.
Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
11 Then spoke the priests and the prophets to the officials and to all the people, saying, "This man is worthy of death; for he has prophesied against this city, as you have heard with your ears."
Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
12 Then Jeremiah spoke to all the officials and to all the people, saying, "YHWH sent me to prophesy against this house and against this city all the words that you have heard.
Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
13 Now therefore amend your ways and your doings, and obey the voice of YHWH your God; and YHWH will relent of the disaster that he has pronounced against you.
Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
14 But as for me, look, I am in your hands; do with me as is good and right in your eyes.
Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
15 Only know for certain that, if you put me to death, you will bring innocent blood on yourselves, and on this city, and on its inhabitants; for of a truth YHWH has sent me to you to speak all these words in your ears."
Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
16 Then the officials and all the people said to the priests and to the prophets: "This man is not worthy of death; for he has spoken to us in the name of YHWH our God."
Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
17 Then rose up certain of the elders of the land, and spoke to all the assembly of the people, saying,
Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
18 "Micah the Morashtite prophesied in the days of Hezekiah king of Judah; and he spoke to all the people of Judah, saying, 'Thus says YHWH of hosts: "Zion shall be plowed as a field, and Jerusalem shall become heaps, and the mountain of the house as the high places of a forest."'
“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
19 Did Hezekiah king of Judah and all Judah put him to death? Did he not fear YHWH, and seek the favor of YHWH, and YHWH relented of the disaster which he had pronounced against them? Thus should we commit great evil against our own souls.
Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
20 "There was also a man who prophesied in the name of YHWH, Uriah the son of Shemaiah of Kiriath Jearim; and he prophesied against this city and against this land according to all the words of Jeremiah.
(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
21 And when Jehoiakim the king, with all his mighty men, and all the officials, heard his words, the king sought to put him to death; but when Uriah heard it, he was afraid, and fled, and went into Egypt.
Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
22 And Jehoiakim the king sent men into Egypt, Elnathan the son of Achbor, and certain men with him, into Egypt;
Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
23 and they fetched forth Uriah out of Egypt, and brought him to Jehoiakim the king, who killed him with the sword, and cast his dead body into the graves of the common people."
Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
24 But the hand of Ahikam the son of Shaphan was with Jeremiah, that they should not give him into the hand of the people to put him to death.
Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.

< Jeremiah 26 >