< Isaiah 8 >

1 YHWH said to me, "Take a large tablet, and write on it with a man's pen, 'For Maher Shalal Hash Baz;'
Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
2 and I will take for myself faithful witnesses to testify: Uriah the priest, and Zechariah the son of Berechiah."
Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 I went to the prophetess, and she conceived, and bore a son. Then said YHWH to me, "Call his name 'Maher Shalal Hash Baz.'
Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
4 For before the child knows how to say, 'My father,' and, 'My mother,' the riches of Damascus and the spoil of Samaria will be carried away by the king of Assyria."
Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 YHWH spoke to me yet again, saying,
Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 "Because this people have refused the waters of Shiloah that go softly, and rejoice in Rezin and Remaliah's son;
“Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
7 now therefore, look, YHWH brings upon them the mighty flood waters of the River: the king of Assyria and all his glory. It will come up over all its channels, and go over all its banks.
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
8 It will sweep onward into Judah. It will overflow and pass through; it will reach even to the neck; and the stretching out of its wings will fill the breadth of your land, Immanuel.
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
9 Make an uproar, you peoples, and be broken in pieces. Listen, all you from far countries. Prepare for battle, and be shattered.
Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Take counsel together, and it will be brought to nothing; speak the word, and it will not stand: for God is with us."
Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
11 For YHWH spoke thus to me with a strong hand, and instructed me not to walk in the way of this people, saying,
Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 "Do not say, 'A conspiracy.' concerning all about which this people say, 'A conspiracy.' And do not fear what they fear, nor be in dread.
“Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
13 YHWH of hosts is who you must regard as holy. He is the one you must fear. He is the one you must dread.
Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 And he will be a sanctuary; but for a stone of stumbling and for a rock that makes them fall to both the houses of Israel, for a trap and for a snare to the inhabitants of Jerusalem.
ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 Many will stumble over it, fall, be broken, be snared, and be captured."
Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
16 Wrap up the testimony. Seal the law among my disciples.
Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 I will wait for YHWH, who hides his face from the house of Jacob, and I will trust in him.
Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
18 Look, I and the children whom God has given me are for signs and wonders in Israel from YHWH of hosts, who dwells on Mount Zion.
Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
19 When they tell you, "Consult with the spirits of the dead and familiar spirits who chirp and who mutter. Shouldn't a people consult with their gods, by consulting the dead on behalf of the living?"
Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
20 Turn to the law and to the testimony. If they do not speak according to this word, surely there is no morning for them.
kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
21 They will pass through it, greatly distressed and hungry; and it will happen that when they are hungry, they will worry, and curse by their king and by their God. They will turn their faces upward,
Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
22 and look to the earth, and see distress, darkness, and the gloom of anguish. They will be driven into thick darkness.
Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.

< Isaiah 8 >