< Genesis 8 >

1 And God remembered Noah, and all the wild animals, and all the tame animals, and all the flying creatures, and all the crawling creatures that were with him in the ship; and God made a wind to pass over the earth, and the waters began to recede.
Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
2 And the fountains of the deep and the floodgates of the sky were closed, and the rain from the sky was restrained.
Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
3 And the waters receded steadily from the land. And after the end of one hundred fifty days the waters had decreased significantly.
Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
4 And in the seventh month, on the seventeenth day of the month, the ship came to rest on the mountains of Ararat.
ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
5 The waters receded continually to the tenth month. In the tenth month, on the first day of the month, the tops of the mountains became visible.
Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
6 It happened at the end of forty days, that Noah opened the window of the ship which he had made,
Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
7 and he sent forth a raven. It went back and forth, until the waters had dried up from the earth.
natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
8 Then he sent forth a dove from it, to see if the waters had abated from the surface of the ground,
Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
9 but the dove found no place to rest her foot, and she returned to him into the ship; for the waters were on the surface of the whole earth. He put forth his hand, and took her, and brought her to him into the ship.
Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
10 And he waited yet another seven days; and again he sent forth the dove out of the ship.
Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
11 The dove came back to him at evening, and, look, in her mouth was an olive leaf plucked off. So Noah knew that the waters had abated from the earth.
Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
12 He stayed yet another seven days, and sent forth the dove; and she did not return to him any more.
Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
13 And it happened in the six hundred first year of Noah's life, in the first month, the first day of the month, the waters had dried up from the earth. And Noah removed the covering of the ship and looked out. And look, the surface of the ground was dry.
Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
14 In the second month, on the twenty-seventh day of the month, the earth was dry.
Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
15 God spoke to Noah, saying,
Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
16 "Go out of the ship, you, and your wife, and your sons, and your sons' wives with you.
“Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
17 Bring out with you every living thing that is with you of all flesh, of flying creatures, and animals, and every creature that crawls on the earth, that they may swarm on the earth, and be fruitful and multiply on the earth."
Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
18 And Noah went forth, with his sons, his wife, and his sons' wives with him.
Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
19 And every wild animal, and every tame animal, and every flying creature, and every creature that crawls on the earth, after their families, went out of the ship.
Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
20 Noah built an altar to God, and took of every clean animal, and of every clean flying creature, and offered burnt offerings on the altar.
Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
21 And God smelled the pleasing aroma, and God said in his heart, "I will never again curse the ground because of humankind, even though the inclination of his heart is evil from his youth, nor will I again destroy every living thing, as I have done.
Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
22 While the earth remains, seed time and harvest, and cold and heat, and summer and winter, and day and night shall not cease."
“Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”

< Genesis 8 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark