< Genesis 29 >

1 Then Jacob went on his journey, and came to the land of the people of the east.
Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
2 He looked and saw a well in the field, and look, three flocks of sheep lying there by it. For out of that well they watered the flocks. The stone on the well's mouth was large.
Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
3 Now all the flocks would be gathered there, and they would roll the stone from the well's mouth, and water the sheep, and put the stone again on the well's mouth in its place.
Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
4 Jacob said to them, "My brothers, where are you from?" They said, "We are from Haran."
Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
5 He said to them, "Do you know Laban, the grandson of Nahor?" They said, "We know him."
Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
6 He said to them, "Is it well with him?" They said, "It is well. See, Rachel, his daughter, is coming with the sheep."
Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
7 He said, "Look, it is still the middle of the day, not time to gather the livestock together. Water the sheep, and go, pasture them."
Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
8 They said, "We can't, until all the flocks are gathered together, and they roll the stone from the well's mouth. Then we water the sheep."
Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
9 While he was yet speaking with them, Rachel came with her father's sheep, for she was tending them.
Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
10 It happened, when Jacob saw Rachel the daughter of Laban, his mother's brother, and the sheep of Laban, his mother's brother, that Jacob went over and rolled the stone from the well's mouth and watered the flock of Laban his mother's brother.
Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
11 Jacob kissed Rachel, and wept loudly.
Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
12 Jacob told Rachel that he was her father's brother, and that he was Rebekah's son. She ran and told her father.
Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
13 It happened, when Laban heard the news of Jacob, his sister's son, that he ran to meet Jacob, and embraced him, and kissed him, and brought him to his house. Jacob told Laban all these things.
Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
14 Laban said to him, "Surely you are my bone and my flesh." He lived with him for a month.
Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
15 Laban said to Jacob, "Because you are my brother, should you therefore serve me for nothing? Tell me what your wages should be?"
Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
16 Laban had two daughters. The name of the older was Leah, and the name of the younger was Rachel.
Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
17 Leah looked rather plain, but Rachel was beautiful in form and beautiful in appearance.
Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
18 Jacob loved Rachel. He said, "I will serve you seven years for Rachel, your younger daughter."
Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
19 Laban said, "It is better that I give her to you, than that I should give her to another man. Stay with me."
Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
20 Jacob served seven years for Rachel, and it seemed only a few days to him because of his love for her.
Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
21 Jacob said to Laban, "Give me my wife, for my time is completed, so that I may sleep with her."
Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
22 Laban gathered together all the people of the place, and gave a feast.
Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
23 It happened in the evening, that he took Leah his daughter and brought her to him, and he slept wit her.
Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
24 Laban gave Zilpah his female servant to his daughter Leah as a servant.
Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
25 It happened in the morning that, look, it was Leah. He said to Laban, "What is this you have done to me? Did I not work for you to have Rachel? Why then have you deceived me?"
Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
26 Laban said, "It is not our custom here to give the younger before the firstborn.
Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
27 Finish the week of this one, and I will give you the other also in exchange for the work which you are to serve with me for another seven years."
Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
28 Then Jacob did so, and fulfilled her week. He gave him Rachel his daughter as wife.
Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
29 Laban gave to Rachel his daughter Bilhah, his female servant, to be her servant.
Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
30 So he slept with Rachel also, and he loved Rachel more than Leah. And he worked with him another seven years.
Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
31 YHWH saw that Leah was unloved, so he made her fertile, but Rachel was barren.
Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
32 Leah conceived, and bore a son, and she named him Reuben. For she said, "Because God has looked at my affliction, and given me a son. For now my husband will love me."
Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
33 She conceived again, and bore a son, and said, "Because God has heard that I am unloved, he has therefore given me this son also." So she named him Simeon.
Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
34 She conceived again, and bore a son. She said, "Now this time my husband will become attached to me, since I have given him three sons." Therefore he was named Levi.
Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
35 She conceived again, and bore a son. She said, "This time will I praise God." Therefore she named him Judah. Then she stopped bearing.
Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.

< Genesis 29 >