< Genesis 23 >

1 Sarah lived one hundred twenty-seven years. This was the length of Sarah's life.
Sara anakhala ndi moyo zaka 127.
2 Sarah died in Kiriath Arba (that is, Hebron), in the land of Canaan. Abraham came to mourn for Sarah, and to weep for her.
Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.
3 Abraham rose up from before his dead, and spoke to the sons of Heth, saying,
Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati,
4 "I am a stranger and a foreigner living with you. Give me a possession of a burying-place with you, that I may remove my dead for burial."
“Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”
5 The sons of Heth answered Abraham, saying to him,
Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti,
6 "Hear us, my lord. You are a prince of God among us. Bury your dead in the best of our tombs. None of us will withhold from you his tomb to prevent you from burying your dead."
“Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”
7 Abraham rose up, and bowed himself to the people of the land, to the sons of Heth.
Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja
8 He talked with them, saying, "If you agree that I may remove my dead for burial, hear me, and approach Ephron the son of Zohar for me,
nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari
9 that he may give me the cave of Machpelah, which he owns; it is at the end of his field. For the full price let him give it to me in your presence as a burial place."
kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”
10 Now Ephron was sitting among the sons of Heth. Ephron the Hethite answered Abraham in the hearing of the sons of Heth, even of all who went in at the gate of his city, saying,
Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu
11 "No, my lord, hear me. I give you the field, and I give you the cave that is in it. In the presence of the sons of my people I give it to you. Bury your dead."
nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”
12 Abraham bowed himself down before the people of the land.
Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo
13 He spoke to Ephron in the audience of the people of the land, saying, "But if you will, please hear me. I will give the price of the field. Take it from me, and I will bury my dead there."
ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”
14 Ephron answered Abraham, saying to him,
Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati,
15 "My lord, listen to me. What is a piece of land worth four hundred shekels of silver between me and you? Therefore bury your dead."
“Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”
16 Abraham listened to Ephron. Abraham weighed to Ephron the silver which he had named in the audience of the sons of Heth, four hundred shekels of silver, according to the current merchants' standard.
Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.
17 So the field of Ephron, which was in Machpelah, which was before Mamre, the field, the cave which was in it, and all the trees that were in the field, that were in all of its borders, were deeded
Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa
18 to Abraham as a possession in the presence of the sons of Heth, before all who went in at the gate of his city.
kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo.
19 After this, Abraham buried Sarah his wife in the cave of the field of Machpelah before Mamre (that is, Hebron), in the land of Canaan.
Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani.
20 The field, and the cave that is in it, were deeded to Abraham as a possession for a burial place by the sons of Heth.
Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.

< Genesis 23 >