< Genesis 21 >

1 Now God visited Sarah as he had said, and did to Sarah as he had spoken.
Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera.
2 Sarah conceived, and bore Abraham a son in his old age, at the set time of which God had spoken to him.
Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza.
3 Abraham called his son who was born to him, whom Sarah bore to him, Isaac.
Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera.
4 Abraham circumcised his son, Isaac, when he was eight days old, as God had commanded him.
Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira.
5 Abraham was one hundred years old when his son, Isaac, was born to him.
Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.
6 Sarah said, "God has made me laugh. Everyone who hears will laugh with me."
Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.”
7 She said, "Who would have said to Abraham, that Sarah would nurse children? For I have borne him a son in his old age."
Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”
8 The child grew, and was weaned. Abraham made a great feast on the day that Isaac was weaned.
Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu.
9 Sarah saw the son of Hagar the Egyptian, whom she had borne to Abraham, mocking.
Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka,
10 Therefore she said to Abraham, "Cast out this slave woman and her son. For the son of this slave woman will not be heir with my son, Isaac."
ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”
11 The thing was very grievous in Abraham's sight on account of his son.
Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake.
12 God said to Abraham, "Do not let it be grievous in your sight because of the boy, and because of your slave woman. In all that Sarah says to you, listen to her voice. For from Isaac will your descendants be called.
Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
13 And I will also make a great nation of the son of the slave woman, because he is your offspring."
Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”
14 Abraham rose up early in the morning, and took food and a skin of water, and gave it to Hagar, putting it on her shoulder; and gave her the child, and sent her away. She departed, and wandered in the wilderness of Beersheba.
Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.
15 The water in the skin was gone, and she shoved the boy under one of the shrubs.
Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba.
16 She went and sat down opposite him, a good way off, about a bow shot away. For she said, "Do not let me see the death of the boy." So she sat across from him, and he wept loudly.
Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.
17 And God heard the voice of the boy, and the angel of God called to Hagar from the sky and said to her, "What troubles you, Hagar? Do not be afraid. For God has heard the voice of the boy where he is.
Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo.
18 Get up, lift up the boy, and hold him by your hand. For I will make him a great nation."
Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”
19 God opened her eyes, and she saw a well of water. She went and filled the skin with water and gave the boy a drink.
Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.
20 God was with the boy, and he grew. He lived in the wilderness, and became, as he grew up, an archer.
Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta.
21 He lived in the wilderness of Paran. His mother got a wife for him from the land of Egypt.
Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.
22 It happened at that time, that Abimelech and Phicol the commander of his army spoke to Abraham, saying, "God is with you in all that you do.
Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita.
23 Now, therefore, swear to me here by God that you will not deal falsely with me, nor with my son, nor with my son's son. But according to the kindness that I have done to you, you shall do to me, and to the land in which you have lived as a foreigner."
Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”
24 And Abraham said, "I swear."
Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”
25 Abraham complained to Abimelech because of a water well, which Abimelech's servants had violently taken away.
Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda.
26 Abimelech said, "I do not know who has done this thing. Neither did you tell me, neither did I hear of it, until today."
Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”
27 Abraham took sheep and cattle, and gave them to Abimelech, and the two of them made a covenant.
Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano.
28 Abraham set seven ewe lambs of the flock by themselves.
Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina,
29 Abimelech said to Abraham, "What do these seven ewe lambs which you have set by themselves mean?"
ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”
30 He said, "You shall take these seven ewe lambs from my hand, that it may be a witness to me, that I have dug this well."
Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”
31 Therefore he called that place Beersheba, because they both swore there.
Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.
32 So they made a covenant at Beersheba. Abimelech rose up with Phicol, the commander of his army, and they returned into the land of the Philistines.
Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti.
33 And Abraham planted a tamarisk tree in Beersheba, and called there on the name of YHWH, the Everlasting God.
Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya.
34 Abraham lived as a foreigner in the land of the Philistines many days.
Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.

< Genesis 21 >