< Ezekiel 38 >

1 The word of YHWH came to me, saying,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 "Son of man, set your face toward Gog, of the land of Magog, the chief prince of Meshech and Tubal, and prophesy against him,
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 and say, 'Thus says YHWH: "Look, I am against you, Gog, chief prince of Meshech and Tubal:
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 and I will turn you around, and put hooks into your jaws, and I will bring you out, with all your army, horses and horsemen, all of them clothed in full armor, a great company with buckler and shield, all of them armed with swords;
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Persia, Ethiopia, and Put with them, all of them with shield and helmet;
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gomer, and all his troops; the house of Togarmah in the uttermost parts of the north, and all his hordes; even many peoples with you.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 "'"Be ready and stay ready, you and all your companies who are assembled to you, and be a guard to them.
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 After many days you shall be summoned: in the latter years you shall come to a land that is restored from war, a gathering from many peoples on the mountains of Israel, that had long been in ruins. Its people were brought out from the peoples, and all of them now live securely.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 You shall advance, coming like a storm. You will be like a cloud covering the land, you, all your troops, and the many other peoples with you."
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 "'Thus says YHWH: "It shall happen on that day, that thoughts shall come into your mind, and you shall devise an an evil scheme:
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 and you shall say, 'I will go up to the land of unwalled villages; I will go to those who who dwell securely, all of them dwelling without walls, and having neither bars nor gates;
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 to seize spoil and carry off plunder; to turn my hand against the waste places that are now inhabited, acquired livestock and goods, who live at the center of the earth.'
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Sheba, and Dedan, and the merchants of Tarshish, with all its young warriors will say to you, 'Have you assembled your armies to carry off plunder, to carry away silver and gold, to take away cattle and goods, to to seize great spoil?'"'
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 "Therefore, son of man, prophesy, and tell Gog, 'Thus says YHWH: "On that day when my people Israel are dwelling securely, you will take notice?
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 You shall come from your place out of the uttermost parts of the north, you and many peoples with you, all of them riding on horses, a great company and a mighty army;
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 and you shall come up against my people Israel, as a cloud covering the land. But when this happens in future days, I will bring you against my land, so that the nations may know me, Gog, when through you I show my holiness in their sight."
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 "'Thus says YHWH: "Are you the one of whom I spoke in former days by my servants the prophets of Israel, who in those days prophesied for years that I would bring you against them?"
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 But it shall happen on that day, when Gog shall come against the land of Israel,' says YHWH, 'that my hot anger will be aroused.
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 For in my zeal, in the fire of my fury, I declare that on that day there shall be a great shaking in the land of Israel;
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 so that the fish of the sea, and the birds of the sky, and the animals of the field, and all crawling creatures who crawl on the land, and all people who are on the face of the earth, shall shake at my presence. And the mountains shall be thrown down, and the cliffs shall fall, and every wall shall fall to the ground.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 I will call for a sword against him on all my mountains,' says YHWH: 'every man's sword shall be against his brother.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 With pestilence and with bloodshed I will enter into judgment with him; and I will rain on him, and on his troops, and on the many peoples who are with him, torrential rains and hailstones, fire, and brimstone.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 I will show my greatness and my holiness, and I will make myself known in the sight of many nations. Then they will know that I am YHWH.'
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezekiel 38 >