< Deuteronomy 29 >

1 These are the words of the covenant which YHWH commanded Moses to make with the children of Israel in the land of Moab, besides the covenant which he made with them in Horeb.
Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
2 Moses called to all Israel, and said to them, You have seen all that YHWH did before your eyes in the land of Egypt to Pharaoh, and to all his servants, and to all his land;
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
3 the great trials which your eyes saw, the signs, and those great wonders:
Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
4 but YHWH has not given you a heart to know, and eyes to see, and ears to hear, to this day.
Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
5 I have led you forty years in the wilderness. Your clothes have not worn out on you, and your shoes have not worn out on your feet.
Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
6 You have not eaten bread, neither have you drunk wine or strong drink; that you may know that I am YHWH your God.
Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
7 When you came to this place, Sihon the king of Heshbon, and Og the king of Bashan, came out against us to battle, and we struck them:
Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
8 and we took their land, and gave it for an inheritance to the Reubenites, and to the Gadites, and to the half-tribe of the Manassites.
Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
9 Keep therefore the words of this covenant, and do them, that you may prosper in all that you do.
Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
10 You stand this day all of you before YHWH your God; your heads, your tribes, your elders, and your officers, even all the men of Israel,
Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
11 your little ones, your wives, and your foreigner who is in the midst of your camps, from the one who cuts your wood to the one who draws your water;
pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
12 that you may enter into the covenant of YHWH your God, and into his oath, which YHWH your God makes with you this day,
Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
13 so that he may establish you today as his people, and that he may your God, as he spoke to you and as he swore to your fathers, to Abraham, to Isaac, and to Jacob.
kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
14 Neither with you only do I make this covenant and this oath,
Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
15 but with him who stands here with us this day before YHWH our God, and also with him who is not here with us this day
amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
16 (for you know how we lived in the land of Egypt, and how we came through the midst of the nations through which you passed;
Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
17 and you have seen their abominations, and their idols, wood and stone, silver and gold, which were among them);
Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
18 lest there should be among you man, or woman, or family, or tribe, whose heart turns away this day from YHWH our God, to go to serve the gods of those nations; lest there should be among you a root that bears gall and wormwood;
Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
19 and it happen, when he hears the words of this curse, that he bless himself in his heart, saying, "I shall have peace, though I walk in the stubbornness of my heart, to destroy the moist with the dry."
Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
20 God will not be willing to forgive him, but then the anger of YHWH and his jealousy will burn against that man, and every curse that is written in this book shall rest on him, and YHWH will blot out his name from under heaven.
Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
21 YHWH will set him apart to evil out of all the tribes of Israel, according to all the curses of the covenant that is written in this book of the law.
Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
22 The generation to come, your children who shall rise up after you, and the foreigner who shall come from a far land, shall say, when they see the plagues of that land, and the sicknesses with which YHWH has made it sick;
Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
23 and that the whole land of it is sulfur, salt, and burning, that it is not sown, nor bears, nor any grass grows in it, like the overthrow of Sodom and Gomorrah, Admah and Zeboiim, which YHWH overthrew in his anger, and in his wrath:
Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
24 even all the nations shall say, "Why has YHWH done thus to this land? What does the heat of this great anger mean?"
Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
25 Then men shall say, "Because they forsook the covenant of YHWH, the God of their fathers, which he made with them when he brought them forth out of the land of Egypt,
Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
26 and went and served other gods, and worshiped them, gods that they did not know, and that he had not given to them:
Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
27 therefore the anger of YHWH was kindled against this land, to bring on it all the curse that is written in this book;
Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
28 and YHWH rooted them out of their land in anger, and in wrath, and in great indignation, and cast them into another land, as at this day."
Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
29 The secret things belong to YHWH our God; but the things that are revealed belong to us and to our children forever, that we may do all the words of this law.
Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.

< Deuteronomy 29 >