< Deuteronomy 14 >

1 You are the people of YHWH your God: you shall not cut yourselves, nor make any baldness between your eyes for the dead.
Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
2 For you are a holy people to YHWH your God, and YHWH has chosen you to be a people for his own possession, above all peoples who are on the face of the earth.
pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
3 You shall not eat any abominable thing.
Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
4 These are the animals which you may eat: the ox, the sheep, and the goat,
Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
5 the deer, and the gazelle, and the roebuck, and the wild goat, and the ibex, and the antelope, and the chamois.
mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
6 Every animal that parts the hoof, and has the hoof cloven in two and chews the cud, among the animals, that may you eat.
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
7 Nevertheless these you shall not eat of them that chew the cud, or of those who have the hoof cloven: the camel, and the hare, and the rabbit; because they chew the cud but do not part the hoof, they are unclean to you.
Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
8 The pig, because it has a split hoof, but doesn't chew the cud, is unclean to you: of their flesh you shall not eat, and their carcasses you shall not touch.
Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
9 These you may eat of all that are in the waters: whatever has fins and scales may you eat;
Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 and whatever doesn't have fins and scales you shall not eat; it is unclean to you.
Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
11 Of all clean birds you may eat.
Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
12 But these are they of which you shall not eat: the eagle, and the vulture, and the osprey,
Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
13 and the kite, and the buzzard, and the vulture after its kind,
nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
14 and every raven after its kind,
mtundu uliwonse wa khwangwala,
15 and the ostrich, and the owl, and the seagull, and the hawk after its kind,
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
16 the little owl, and the great owl, and the horned owl,
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
17 and the pelican, and the vulture, and the cormorant,
tsekwe, vuwo, dembo,
18 and the stork, and the heron after its kind, and the hoopoe, and the bat.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
19 All winged crawling creatures are unclean to you: they shall not be eaten.
Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
20 Of all clean birds you may eat.
Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
21 You shall not eat of anything that dies of itself: you may give it to the foreigner living among you who is within your gates, that he may eat it; or you may sell it to a foreigner: for you are a holy people to YHWH your God. You shall not boil a young goat in its mother's milk.
Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
22 You shall surely tithe all the increase of your seed, that which comes forth from the field year by year.
Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
23 You shall eat before YHWH your God, in the place which he shall choose, to cause his name to dwell there, the tithe of your grain, of your new wine, and of your oil, and the firstborn of your herd and of your flock; that you may learn to fear YHWH your God always.
Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
24 If the way is too long for you, so that you are not able to carry it, because the place is too far from you, which YHWH your God shall choose, to set his name there, when YHWH your God shall bless you;
Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
25 then you shall turn it into money, and bind up the money in your hand, and shall go to the place which YHWH your God shall choose:
ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
26 and you shall bestow the money for whatever your soul desires, for cattle, or for sheep, or for wine, or for strong drink, or for whatever your soul asks of you; and you shall eat there before YHWH your God, and you shall rejoice, you and your household.
Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
27 The Levite who is within your gates, you shall not forsake him; for he has no portion nor inheritance with you.
Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
28 At the end of every three years you shall bring forth all the tithe of your increase in the same year, and shall lay it up within your gates:
Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
29 and the Levite, because he has no portion nor inheritance with you, and the foreigner living among you, and the fatherless, and the widow, who are within your gates, shall come, and shall eat and be satisfied; that YHWH your God may bless you in all the work of your hand which you do.
kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

< Deuteronomy 14 >