< Daniel 6 >

1 It pleased Daryavesh to set over the kingdom one hundred twenty satraps, who should be throughout the whole kingdom;
Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
2 and over them three administrators, of whom Daniel was one; that these satraps might give account to them, and that the king might not suffer loss.
ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
3 Then this Daniel was distinguished above the administrators and the satraps, because an extraordinary spirit was in him; and the king thought to set him over the whole realm.
Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
4 Then the administrators and the satraps sought to find a charge against Daniel regarding the kingdom; but they could find no charge or fault, because he was faithful. Neither was there any error or fault found in him.
Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
5 Then these men said, "We will not find any charge against this Daniel, except we find it against him concerning the law of his God."
Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
6 Then these administrators and satraps assembled together to the king, and said this to him, "King Daryavesh, live forever.
Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
7 All the administrators of the kingdom, the deputies and the satraps, the counselors and the governors, have consulted together to establish a royal statute, and to make a strong decree, that whoever shall ask a petition of any god or man for thirty days, except of you, O king, he shall be cast into the den of lions.
Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
8 Now, O king, establish the decree, and sign the writing, that it not be changed, according to the law of the Medes and Persians, which cannot be changed."
Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
9 Therefore king Daryavesh signed the writing and the decree.
Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
10 When Daniel knew that the writing was signed, he went into his house (now his windows were open in his chamber toward Jerusalem) and he kneeled on his knees three times a day, and prayed, and gave thanks before his God, as he did before.
Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
11 Then these men assembled together, and found Daniel making petition and petition before his God.
Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
12 Then they came near, and spoke before the king concerning the king's decree. "Haven't you signed a decree, that every man who shall make petition to any god or man within thirty days, except to you, O king, shall be cast into the den of lions?" The king answered, "The thing is true, according to the law of the Medes and Persians, which cannot be changed."
Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
13 Then they answered and said before the king, "That Daniel, who is of the children of the captivity of Judah, doesn't regard you, O king, nor the decree that you have signed, but makes his petition three times a day."
Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
14 Then the king, when he heard these words, was very displeased, and set his heart on Daniel to deliver him. And he labored until the going down of the sun to rescue him.
Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
15 Then these men assembled together to the king, and said to the king, "Know, O king, that it is a law of the Medes and Persians, that no decree nor statute which the king establishes may be changed."
Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
16 Then the king commanded, and they brought Daniel, and cast him into the den of lions. Now the king spoke and said to Daniel, "Your God whom you serve continually, he will deliver you."
Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
17 A stone was brought, and placed on the opening of the den; and the king sealed it with his own signet, and with the signet of his lords; that nothing might be changed concerning Daniel.
Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
18 Then the king went to his palace, and passed the night fasting; neither were instruments of music brought before him. And his sleep fled from him.
Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
19 Then the king arose very early in the morning, and went in haste to the den of lions.
Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
20 When he came near to the den to Daniel, he cried with a lamentable voice. The king spoke and said to Daniel, "Daniel, servant of the living God. Is your God, whom you serve continually, able to deliver you from the lions?"
Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
21 Then said Daniel to the king, "O king, live forever.
Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
22 My God has sent his angel, and has shut the lions' mouths, and they have not hurt me; because before him innocence was found in me; and also before you, O king, have I done no wrong."
Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
23 Then was the king exceedingly glad, and commanded that they should take Daniel up out of the den. So Daniel was taken up out of the den, and no manner of hurt was found on him, because he had trusted in his God.
Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
24 The king commanded, and they brought those men who had accused Daniel, and they cast them into the den of lions, them, their children, and their wives; and the lions overpowered them, and broke all their bones in pieces, before they came to the bottom of the den.
Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
25 Then king Daryavesh wrote to all the peoples, nations, and languages, who dwell in all the earth: "Peace be multiplied to you.
Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
26 I make a decree, that in all the dominion of my kingdom men tremble and fear before the God of Daniel; for he is the living God, and steadfast forever. His kingdom shall not be destroyed; and his dominion shall be to the end.
“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
27 He delivers and rescues, and he works signs and wonders in heaven and in earth, who has delivered Daniel from the power of the lions."
Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
28 So this Daniel prospered in the reign of Daryavesh, and in the reign of Koresh the Persian.
Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.

< Daniel 6 >