< Amos 2 >

1 Thus says YHWH: "For three transgressions of Moab, yes, for four, I will not turn away its punishment; because he burned the bones of the king of Edom into lime;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 but I will send a fire on Moab, and it will devour the palaces of Kerioth; and Moab will die with tumult, with shouting, and with the sound of the trumpet;
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 and I will cut off the judge from their midst, and will kill all its officials with him," says YHWH.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 Thus says YHWH: "For three transgressions of Judah, yes, for four, I will not turn away its punishment; because they have rejected YHWH's law, and have not kept his statutes. Their false idols which they made, after which their fathers walked, have led them astray.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 But I will send a fire on Judah, and it will devour the palaces of Jerusalem."
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 Thus says YHWH: "For three transgressions of Israel, yes, for four, I will not turn away its punishment; because they have sold the righteous for silver, and the needy for a pair of shoes;
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 They trample on the dust of the earth on the head of the poor, and deny justice to the oppressed; and a man and his father use the same maiden, to profane my holy name;
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 and they lay themselves down beside every altar on clothes taken in pledge; and in the house of their God they drink the wine of those who have been fined.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 Yet I destroyed the Amorite before them, whose height was like the height of the cedars, and he was strong as the oaks; yet I destroyed his fruit from above, and his roots from beneath.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 Also I brought you up out of the land of Egypt, and led you forty years in the wilderness, to possess the land of the Amorite.
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 I raised up some of your sons for prophets, and some of your young men for Nazirites. Isn't this true, you children of Israel?" says YHWH.
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 "But you gave the Nazirites wine to drink, and commanded the prophets, saying, 'Do not prophesy.'
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 Look, I will crush you in your place, as a cart crushes that is full of grain.
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 Flight will perish from the swift; and the strong won't strengthen his force; neither shall the mighty deliver himself;
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 neither shall he stand who handles the bow; and he who is swift of foot won't escape; neither shall he who rides the horse deliver himself;
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 and he who is courageous among the mighty will flee away naked on that day," says YHWH.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.

< Amos 2 >