< 2 Samuel 22 >

1 David spoke to YHWH the words of this song in the day that YHWH delivered him out of the hand of all his enemies, and out of the hand of Saul:
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 and he said, "YHWH is my Rock, and my fortress, and my deliverer.
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 My God, my Rock, in him I will take refuge, my shield, and the horn of my salvation, my high tower, and my refuge, my savior; from violent people he saves me.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 I call on YHWH, who is worthy to be praised, and I am saved from my enemies.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 For the waves of death surrounded me, and the currents of ungodliness overwhelmed me.
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 The cords of Sheol were around me. The snares of death caught me. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
7 In my distress I called upon YHWH, and I cried out to my God. He heard my voice out of his temple, and my cry came into his ears.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 Then the earth shook and trembled. The foundations of the mountains quaked and were shaken, because he was angry.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 Smoke went up out of his nostrils. Fire out of his mouth devoured. Coals were kindled by it.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 He bowed the heavens also, and came down. Thick darkness was under his feet.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 He rode on a cherub, and flew; and he soared on the wings of the wind.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 He made darkness his hiding place, his canopy around him thick clouds dark with water.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 From the brightness before him his thick clouds passed on, with hailstones and coals of fire.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 YHWH thundered from heaven. The Most High uttered his voice.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 And he sent out arrows and scattered them, and he shot lightning bolts and routed them.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 Then the channels of the sea appeared. The foundations of the world were laid bare by the rebuke of YHWH, at the blast of the breath of his nostrils.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 He sent from on high and he took me. He drew me out of many waters.
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 He delivered me from my strong enemy, from those who hated me, for they were too mighty for me.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 They came on me in the day of my calamity, but YHWH was my support.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 He also brought me out into a large place. He delivered me, because he delighted in me.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 YHWH rewarded me according to my righteousness. He rewarded me according to the cleanness of my hands.
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 For I have kept the ways of YHWH, and have not wickedly departed from my God.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 For all his ordinances were before me, and his statutes I did not put away from me.
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 I was also perfect toward him. I kept myself from my iniquity.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 Therefore YHWH has rewarded me according to my righteousness, according to the cleanness of my hands in his sight.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 With the faithful you show yourself faithful. With the innocent you show yourself innocent.
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 With the pure you show yourself pure. And with the crooked you show yourself tortuous.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 You save a humble people, but the eyes of the proud you will bring low.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 For you light my lamp. YHWH my God lights up my darkness.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 For by you, I run against a troop. By my God, I leap over a wall.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 As for God, his way is perfect. The word of YHWH is pure. He is a shield to all those who take refuge in him.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 For who is God, besides YHWH? Who is a rock, besides our God,
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 the God who girds me with strength, and makes my way blameless?
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 He makes my feet like those of a deer, and sets me on my high places.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 He teaches my hands to war, so that my arms bend a bow of bronze.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 You have also given me the shield of your salvation, and your right hand holds me up, and your help has made me great.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 You have enlarged my steps under me. My feet have not slipped.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 I pursued my enemies and overtook them, and I did not turn back until they were destroyed.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 And I consumed them, and struck them through, so that they did not rise. And they fell beneath my feet.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 For you have equipped me with strength for the battle. You have subdued under me those who rose up against me.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 You have also made my enemies turn their backs to me, that I might cut off those who hate me.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 They cry out, but there was none to save; even to YHWH, but he did not answer them.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 Then I ground them as fine as the dust on the surface of a path. Like the mud in the streets, I trampled them.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 You also have delivered me from the strivings of my people. You have kept me to be the head of the nations. A people whom I have not known will serve me.
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 As soon as they hear of me they obey me. Foreigners come cringing to me;
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 they are not bound in chains.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 YHWH lives. Blessed be my rock. Exalted be God, the rock of my salvation,
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 even the God who executes vengeance for me, and subdues peoples under me,
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 who brings me away from my enemies. Yes, you lift me up above those who rise up against me. You protect me from the violent man.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Therefore I will praise you, YHWH, among the nations, and will sing praises to your name.
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 He gives great deliverance to his king, and shows loving kindness to his anointed, to David and to his descendants, until forever."
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< 2 Samuel 22 >