< 2 Samuel 12 >

1 So YHWH sent Nathan to David. And he came to him, and said to him, "Tell me how you judge this case. There were two men in a certain city, the one rich and the other poor.
Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
2 The rich man had very many flocks and herds,
Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
3 but the poor man had nothing, except one little ewe lamb, which he had aquired. And he raised it and it grew up alongside him and his children. It used to eat of his morsel and drink from his cup and sleep in his arms, and it was like a daughter to him.
koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
4 Now a traveler came to the rich man, but he was unwilling to take from his own flock or his own herd to prepare for the traveler who had come to him, but took the poor man's lamb and prepared it for the man who had come to him."
“Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
5 Then David became very angry with that man, and he said to Nathan, "As YHWH lives, the man who has done this deserves death.
Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
6 He must restore the lamb fourfold, because he did this thing, and because he had no pity."
Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
7 Then Nathan said to David, "You are the man. This is what YHWH, the God of Israel, says: 'I anointed you king over Israel, and I delivered you out of the hand of Saul.
Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
8 I gave you your master's house, and your master's wives into your care, and gave you the house of Israel and of Judah; and if that would have been too little, I would have added to you many more such things.
Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
9 Why have you despised YHWH, to do that which is evil in his sight? You have struck Uriah the Hethite with the sword, and have taken his wife to be your wife, and have slain him with the sword of the people of Ammon.
Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
10 Now therefore the sword will never depart from your house, because you have despised me, and have taken the wife of Uriah the Hethite to be your wife.'
Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
11 "This is what YHWH says: 'Look, I will raise up evil against you out of your own house; and I will take your wives before your eyes, and give them to your neighbor, and he will lie with your wives in the sight of this sun.
“Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
12 For you did it secretly, but I will do this thing before all Israel, and before the sun.'"
Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
13 David said to Nathan, "I have sinned against YHWH." Nathan said to David, "YHWH also has put away your sin. You will not die.
Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
14 However, because by this deed you have shown utter contempt for YHWH, the child also who is born to you shall surely die."
Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
15 Then Nathan went to his home. And God struck the child that Uriah's wife bore to David, and it was very sick.
Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
16 Then David sought from God on behalf of the child. And David fasted, and went in and lay all night on the ground.
Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
17 And the elders of his house approached him to lift him up from the ground, but he was unwilling, and he would not eat food with them.
Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
18 It happened on the seventh day, that the child died. The servants of David feared to tell him that the child was dead; for they said, "Look, while the child was yet alive, we spoke to him, and he did not listen to our voice. How will he then harm himself, if we tell him that the child is dead?"
Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
19 But when David noticed that his servants were whispering together, David perceived that the child was dead; and David said to his servants, "Is the child dead?" They said, "He is dead."
Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
20 Then David arose from the ground, and washed, and anointed himself, and changed his clothing; and he came into the house of YHWH, and worshiped. Then he went to his own house, and he asked for bread to eat. And they set bread before him, and he ate.
Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
21 Then his servants said to him, "What is this that you have done? You fasted and wept and kept vigil for the child while he was alive; but when the child was dead, you rose up and ate bread."
Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
22 He said, "While the child was yet alive, I fasted and wept; for I said, 'Who knows whether YHWH will not be gracious to me, that the child may live?'
Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
23 But now he is dead, why should I fast? Can I bring him back? I shall go to him, but he will not return to me."
Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
24 David comforted Bathsheba his wife, and went in to her, and lay with her. She bore a son, and he called his name Solomon. YHWH loved him;
Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
25 and he sent by the hand of Nathan the prophet; and he named him Jedidiah, for YHWH's sake.
Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
26 Now Joab fought against Rabbah of the people of Ammon, and took the royal city.
Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
27 Joab sent messengers to David, and said, "I have fought against Rabbah, and have also taken the water supply of the city.
Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
28 Now therefore gather the rest of the people together, and besiege the city and capture it yourself, or I will capture the city, and it will be named after me."
Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
29 David gathered all the people together, and went to Rabbah, and fought against it, and took it.
Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
30 He took the crown of their king from off his head; and its weight was a talent of gold, and in it were precious stones; and it was set on David's head. He brought out the spoil of the city, a very great amount.
Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
31 He brought out the people who were in it, and put them to work with saws, and iron picks, and iron axes, and to labor at the brick kiln. And he did the same to all the cities of the people of Ammon. David and all the people returned to Jerusalem.
ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Samuel 12 >