< 1 Samuel 1 >

1 Now there was a certain man of Ramathaim, a Zuphite of the hill country of Ephraim, and his name was Elkanah, the son of Jeroham, the son of Elihu, the son of Toah, the son of Zuph, an Ephraimite.
Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
2 And he had two wives; the name of the one was Hannah, and the name of the other, Peninnah. And Peninnah had children, but Hannah had no children.
Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 This man went up out of his city from year to year to worship and to sacrifice to YHWH of hosts in Shiloh. The two sons of Eli, Hophni and Phinehas, priests of YHWH, were there.
Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
4 When the day came for Elkanah to sacrifice, he would give portions to his wife Peninnah and to all her sons and her daughters.
Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
5 But to Hannah he would give a double portion because he loved Hannah. Now YHWH had kept her from conceiving.
Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
6 And because YHWH kept her from conceiving, her rival used to taunt her severely, to irritate her.
Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
7 And this went on year after year, as often as she went up to the house of YHWH, she taunted her; therefore she would weep and refuse to eat.
Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
8 And her husband Elkanah said to her, "Hannah, why are you weeping? And why are you not eating? And why are you so sad? Am I not better to you than ten sons?"
Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 So Hannah got up after eating and drinking in Shiloh, and stood before YHWH. Now Eli the priest was sitting on the seat by the doorpost of the temple of YHWH.
Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
10 And she was greatly distressed and prayed to YHWH, and wept uncontrollably.
Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
11 And she vowed a vow and said, "YHWH of hosts, if you will indeed look on the affliction of your servant and remember me and not forget your servant, but will give to your servant a son, then I will set him before you as a Nazirite until the day of his death. And he will not drink wine or strong drink, and no razor will come on his head."
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 Now it happened, as she continued praying before YHWH, that Eli observed her mouth.
Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
13 And she was speaking in her heart; only her lips moved, but her voice was not heard. Therefore Eli thought she was drunk.
Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
14 So Eli said to her, "How long will you make yourself drunk? Put away your wine, and go from before YHWH."
Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 And Hannah answered, "No, my lord, I am a woman of a sorrowful spirit. I have drunk neither wine nor strong drink, but I poured out my soul before YHWH.
Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
16 Do not count your servant as a worthless woman; for I have been speaking out of the abundance of my distress and my anguish."
Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 Then Eli answered, "Go in peace; and may the God of Israel grant your petition that you have asked of him."
Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 She said, "Let your servant find favor in your sight." So the woman went her way, and entered her quarters, and ate; and her facial expression wasn't sad any more.
Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 They rose up in the morning early, and worshiped before YHWH, and returned, and came to their house to Ramah: and Elkanah knew Hannah his wife; and YHWH remembered her.
Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
20 It happened, when the time had come, that Hannah conceived, and bore a son; and she named him Samuel, saying, "Because I have asked him of YHWH."
Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
21 The man Elkanah, and all his house, went up to offer to YHWH the yearly sacrifice, and to redeem his vow and all the tithes of his land.
Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
22 But Hannah did not go up; for she said to her husband, "Not until the child is weaned; then I will bring him, that he may appear before YHWH, and stay there forever."
Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 Elkanah her husband said to her, "Do what seems good in your eyes. Wait until you have weaned him; only may YHWH establish what you have said." So the woman waited and nursed her son, until she weaned him.
Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 Then she took him to Shiloh along with a three-year old bull, and bread, and an ephah of flour, and a skin of wine. And she came to the house of YHWH in Shiloh, and the boy was with them. And they went before YHWH and his father slaughtered the sacrifice, which he did annually to YHWH. Then he brought the boy,
Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
25 and he slaughtered the bull. And Hannah, the mother of the boy, brought him to Eli.
Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
26 She said, "Oh, my lord, as your soul lives, my lord, I am the woman who stood by you here, praying to YHWH.
Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
27 For this child I prayed; and YHWH has given me my petition which I asked of him.
Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
28 Therefore also I have lent him to YHWH. As long as he lives he is lent to YHWH." Then she left him there, and she worshipped before YHWH.
Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.

< 1 Samuel 1 >