< 1 Samuel 19 >

1 Saul spoke to Jonathan his son, and to all his servants, that they should kill David. But Saul's son Jonathan liked David very much.
Sauli anawuza mwana wake Yonatani ndi nduna zake zonse kuti aphe Davide. Koma Yonatani amamukonda kwambiri Davide.
2 So Jonathan told David, saying, "Saul seeks to kill you. Please take care of yourself in the morning, and keep hidden in a secret place.
Choncho anawuza Davide kuti, “Abambo anga Sauli akufuna kukupha. Tsono uchenjere. Mmawa upite ukabisale ndipo ukakhale komweko.
3 I will go out and stand beside my father in the field where you are, and I will talk with my father about you; and if I see anything, I will tell you."
Ine ndidzapita ndi kukayima pafupi ndi abambo anga ku munda kumene iwe ukabisale. Ndipo ndidzayankhula ndi abambo anga za iwe ndipo chilichonse chimene ndikamve ndidzakuwuza.”
4 Jonathan spoke good of David to Saul his father, and said to him, "Do not let the king sin against his servant, against David; because he has not sinned against you, and because his works have been very good toward you;
Tsono Yonatani anakanena zabwino za Davide kwa abambo ake Sauli ndipo anati, “Mfumu musachimwire mtumiki wanu Davide, sanakuchimwireni, koma amakuchitirani zabwino kwambiri.
5 for he put his life in his hand, and struck the Philistine, and YHWH worked a great victory for all Israel. You saw it, and rejoiced. Why then will you sin against innocent blood, to kill David without a cause?"
Iye anayika moyo wake pa chiswe pamene anapha Mfilisiti uja. Choncho Yehova anachita zazikulu popambanitsa Aisraeli pa nkhondo. Inu munaona zonsezo ndipo munakondwera. Nanga nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwira munthu wosalakwa pofuna kupha Davide?”
6 Saul listened to the voice of Jonathan, and Saul swore, "As YHWH lives, he shall not be put to death."
Sauli anamvera mawu a Yonatani ndipo analumbira kuti, “Pali Yehova, Davide sadzaphedwa.”
7 Jonathan called David, and Jonathan showed him all those things. Jonathan brought David to Saul, and he was in his presence, as before.
Pambuyo pake Yonatani anayitana Davide namuwuza zonsezi. Choncho Yonatani anabwera naye Davide kwa Sauli ndipo ankamutumikira Sauliyo monga kale.
8 There was war again. David went out, and fought with the Philistines, and killed them with a great slaughter; and they fled before him.
Panabukanso nkhondo ina ndipo Davide anapita ndi kukamenyana ndi Afilisti. Iye anawakantha mwamphamvu kotero kuti Afilisti anathawa.
9 An evil spirit from YHWH was on Saul, as he sat in his house with his spear in his hand; and David was playing with his hand.
Tsiku lina mzimu woyipa uja unafikanso pa Sauli. Nthawi imeneyi nʼkuti Sauli uja ali mʼnyumba mwake, mkondo uli mʼdzanja lake ndi Davide akuyimba zeze,
10 Saul sought to pin David even to the wall with the spear; but he slipped away out of Saul's presence, and he stuck the spear into the wall. David fled, and escaped that night.
Sauli anafuna kumubaya Davide ndi kumukhomera kukhoma, koma Davide anapewa mkondowo kotero Sauli anakabaya pa khoma. Usiku womwewo Davide anathawa.
11 Saul sent messengers to David's house, to watch him, and to kill him in the morning. Mikal, David's wife, told him, saying, "If you do not save your life tonight, tomorrow you will be killed."
Usiku womwewo Sauli anatumiza anthu ku nyumba ya Davide kuti akamubisalire ndi kumupha mmamawa. Koma Mikala mkazi wake anamuchenjeza nati, “Ngati usiku uno supulumutsa moyo wako, mawa udzaphedwa.”
12 So Mikal let David down through the window. He went, fled, and escaped.
Choncho Mikala anamutulutsira Davide pa zenera, ndipo anathawa ndi kupulumuka.
13 Mikal took the teraphim, and laid it in the bed, and put a pillow of goats' hair at its head, and covered it with the clothes.
Kenaka Mikala anatenga fano naligoneka pa bedi nayika pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwa fanolo ndipo analifunditsa nsalu.
14 When Saul sent messengers to take David, she said, "He is sick."
Pamene amithenga a Sauli aja anafika kuti akamugwire Davide, Mikala anati, “Davide akudwala.”
15 Then he sent the messengers to see David, saying, "Bring him up to me in the bed, that I may kill him."
Koma Sauli anatumanso anthuwo kuti akamuone Davide, nati, “Mubwere naye kuno ali pa bedi pomwepo kuti ndidzamuphe.”
16 When the messengers came in, look, the teraphim was in the bed, with the pillow of goats' hair at its head.
Koma pamene anthuwo analowa, anangoona fano pa bedipo ndi pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwake.
17 Saul said to Mikal, "Why have you deceived me thus, and let my enemy go, so that he is escaped?" Mikal answered Saul, "He said, 'Let me go. Why should I kill you?'"
Tsono Sauli anafunsa Mikala kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandinamiza chotere polola kuti mdani wanga athawe?” Mikala anayankha kuti, “Davide anandiwuza kuti, ‘Ukapanda kutero ndikupha.’”
18 Now David fled, and escaped, and came to Samuel to Ramah, and told him all that Saul had done to him. And he and Samuel went and lived in the dwellings.
Choncho Davide anathawa napulumuka. Pambuyo pake anapita kwa Samueli ku Rama nakamuwuza zonse zimene Sauli anamuchita. Kenaka iye ndi Samueli anapita kukakhala ku Nayoti.
19 And it was told to Saul, saying, "Look, David is in the dwellings at Ramah."
Sauli anamva kuti, “Davide ali ku Nayoti ku Rama.”
20 And Saul sent messengers to capture David. But when they saw a company of the prophets prophesying, and Samuel standing as head over them, the Spirit of God came upon the messengers of Saul, and they prophesied.
Choncho iye anatumiza anthu kuti akamugwire Davide. Koma anaona gulu la aneneri likulosera ndi Samueli akuwatsogolera. Pomwepo Mzimu wa Mulungu unawafikira ndipo nawonso anayamba kulosera.
21 When it was told to Saul, he sent other messengers, and they also prophesied. Saul sent messengers again the third time, and they also prophesied.
Sauli atamva zimenezi anatumizanso anthu ena, koma nawonso anayamba kulosa. Anatumanso anthu ena kachitatu, koma nawonso anayamba kulosa.
22 And Saul became very angry, and he himself also went to Ramah, and came to the cistern of the threshing floor that is on the bare hill. And he asked, "Where are Samuel and David?" And one said, "Look, they are in the dwellings at Ramah."
Pomaliza Sauli mwini wake ananyamuka kupita ku Rama ndipo anafika ku chitsime chachikulu cha ku Seku. Ndipo anafunsa, “Samueli ndi Davide ali kuti?” Munthu wina anamuyankha kuti, “Ali ku Nayoti ku Rama.”
23 So he went to the dwellings at Ramah. Then the Spirit of God came on him also, and he went on, and prophesied, until he came to the dwellings in Ramah.
Choncho Sauli anapita ku Nayoti ku Rama. Koma Mzimu wa Mulungu unafikanso pa iye ndipo ankalosa akuyenda mpaka anafika ku Nayoti.
24 And he stripped off his clothes and prophesied before them, and lay down naked all that day and all that night. Thus it is said, "Is Saul also among the prophets?"
Nayenso anavula zovala zake nayamba kulosa pamaso pa Samueli. Kenaka anagona wamaliseche tsiku lonse ndi usiku wonse. Nʼchifukwa chake anthu amati, “Kodi Sauli alinso mmodzi wa aneneri?”

< 1 Samuel 19 >