< 1 Kings 13 >

1 Look, there came a man of God out of Judah by the word of YHWH to Beth El: and Jeroboam was standing by the altar to burn incense.
Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
2 He cried against the altar by the word of YHWH, and said, "Altar, altar, thus says YHWH: 'Look, a son shall be born to the house of David, Josiah by name. On you he shall sacrifice the priests of the high places who burn incense on you, and they will burn men's bones on you.'"
Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
3 He gave a sign the same day, saying, "This is the sign which YHWH has spoken: Look, the altar will be split apart, and the ashes that are on it will be poured out."
Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
4 It happened, when the king heard the saying of the man of God, which he cried against the altar in Bethel, that Jeroboam put out his hand from the altar, saying, "Seize him." His hand, which he put out against him, dried up, so that he could not draw it back again to himself.
Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
5 The altar also was split apart, and the ashes poured out from the altar, according to the sign which the man of God had given by the word of YHWH.
Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
6 The king answered the man of God, "Now plead for the favor of YHWH your God, and pray for me, that my hand may be restored me again." The man of God entreated YHWH, and the king's hand was restored him again, and became as it was before.
Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
7 The king said to the man of God, "Come home with me, and refresh yourself, and I will give you a reward."
Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
8 The man of God said to the king, "Even if you gave me half of your house, I would not go in with you, neither would I eat bread nor drink water in this place;
Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
9 for so was it commanded me by the word of YHWH, saying, 'You shall eat no bread, nor drink water, neither return by the way that you came.'"
Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
10 So he went another way, and did not return by the way that he came to Bethel.
Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
11 Now there lived an old prophet in Bethel; and one of his sons came and told him all the works that the man of God had done that day in Bethel. And they also told their father the words which he had spoken to the king.
Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
12 Their father said to them, "Which way did he go?" Now his sons showed him the way the man of God went, who came from Judah.
Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
13 He said to his sons, "Saddle the donkey for me." So they saddled the donkey for him; and he rode on it.
Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
14 He went after the man of God, and found him sitting under an oak. He said to him, "Are you the man of God who came from Judah?" He said, "I am."
ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
15 Then he said to him, "Come home with me, and eat bread."
Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
16 He said, "I may not return with you, nor go in with you; neither will I eat bread nor drink water with you in this place.
Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
17 For it was said to me by the word of YHWH, 'You shall eat no bread nor drink water there, nor turn again to go by the way that you came.'"
Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
18 He said to him, "I also am a prophet as you are; and an angel spoke to me by the word of YHWH, saying, 'Bring him back with you into your house, that he may eat bread and drink water.'" He lied to him.
Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
19 So he went back with him, and ate bread in his house, and drank water.
Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
20 It happened, as they sat at the table, that the word of YHWH came to the prophet who brought him back;
Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
21 and he cried to the man of God who came from Judah, saying, "Thus says YHWH, 'Because you have been disobedient to the mouth of YHWH, and have not kept the commandment which YHWH your God commanded you,
Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
22 but came back, and have eaten bread and drunk water in the place of which he said to you, "Eat no bread, and drink no water"; your body shall not come to the tomb of your fathers.'"
Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
23 It happened, after he had eaten bread, and after he had drunk, that he saddled the donkey for the prophet whom he had brought back.
Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
24 When he had gone, a lion met him by the way, and killed him. His body was cast in the way, and the donkey stood by it. The lion also stood by the body.
Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
25 Look, men passed by, and saw the body cast in the way, and the lion standing by the body; and they came and told it in the city where the old prophet lived.
Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
26 When the prophet who brought him back from the way heard of it, he said, "It is the man of God who was disobedient to the mouth of YHWH. Therefore YHWH has delivered him to the lion, which has mauled him and slain him, according to the word of YHWH, which he spoke to him."
Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
27 He spoke to his sons, saying, "Saddle the donkey for me." They saddled it.
Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
28 He went and found his body cast in the way, and the donkey and the lion standing by the body. The lion had not eaten the body, nor mauled the donkey.
Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
29 The prophet took up the body of the man of God, and laid it on the donkey, and brought it back. And he came to the city of the old prophet to mourn and to bury him.
Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
30 He laid his body in his own grave; and they mourned over him, saying, "Alas, my brother."
Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
31 It happened, after he had buried him, that he spoke to his sons, saying, "When I am dead, then bury me in the tomb in which the man of God is buried. Lay my bones beside his bones.
Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
32 For the saying which he proclaimed by the word of YHWH against the altar in Bethel, and against all the houses of the high places which are in the cities of Samaria, will surely happen."
Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
33 After this thing Jeroboam did not return from his evil way, but again made priests of the high places from among all the people. He consecrated anyone who wanted to be a priest at the high places.
Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
34 This thing became sin to the house of Jeroboam, even to cut it off, and to destroy it from off the surface of the earth.
Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.

< 1 Kings 13 >