< 1 Chronicles 11 >
1 Then all Israel gathered together to David at Hebron, saying, "Look, we are your bone and your flesh.
Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife abale anu.
2 In times past, even when Saul was king, it was you who led out and brought in Israel. YHWH your God said to you, 'You shall be shepherd of my people Israel, and you shall rule over my people Israel.'"
Kale lija, ngakhale pamene Sauli anali mfumu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwuzani kuti, ‘Iwe udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
3 So all the elders of Israel came to the king to Hebron; and David made a covenant with them in Hebron before YHWH; and they anointed David king over Israel, according to the word of YHWH by Samuel.
Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, iye anachita nawo pangano pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli, monga momwe Yehova analonjezera kudzera mwa Samueli.
4 David and all Israel went to Jerusalem (that is, Jebus); and the Jebusites, the inhabitants of the land, were there.
Davide ndi Aisraeli onse anapita ku Yerusalemu (ku Yebusi). Ayebusi amene ankakhala kumeneko
5 The inhabitants of Jebus said to David, "You shall not come in here." Nevertheless David took the stronghold of Zion, that is, the City of David.
anamuwuza Davide kuti, “Simulowa muno.” Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
6 David said, "Whoever strikes the Jebusites first shall be chief and captain." Joab the son of Zeruiah went up first, and was made chief.
Davide anali atanena kuti “Aliyense amene adzatsogolere kukathira nkhondo Ayebusi adzakhala mkulu wa asilikali.” Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anayamba kupita, motero anakhala mkulu wa asilikali.
7 David lived in the stronghold; therefore they called it the City of David.
Tsono Davide anakhazikika mu lingamo, ndipo mzindawu anawutcha Mzinda wa Davide.
8 He built the city all around, from the Millo even around; and Joab repaired the rest of the city.
Iye anamanga malo onse ozungulira, kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. Ndipo Yowabu anakonzanso mbali ina ya mzindawu.
9 David grew greater and greater; for YHWH of hosts was with him.
Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Wamphamvuzonse.
10 Now these are the chief of the warriors whom David had, who gave him strong support in his kingdom, together with all Israel, to make him king, according to the word of YHWH concerning Israel.
Awa ndiye anali atsogoleri amphamvu a Davide. Iwo pamodzi ndi Aisraeli onse, anathandiza kulimbikitsa ufumu wake kuti ukwanire madera onse, monga momwe Yehova analonjezera.
11 This is the number of the warriors whom David had: Jeshbaal the son of Hachmoni, leader of the Three. And he wielded his spear against eight hundred and killed them at one time.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yasobeamu Mhakimoni anali mkulu wa atsogoleri. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300 nthawi imodzi.
12 After him was Eleazar the son of Dodo, the Ahohite, who was one of the Three warriors.
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi, mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu.
13 He was with David at Pas Dammim, and there the Philistines were gathered together to battle, where there was a plot of ground full of barley; and the people fled from before the Philistines.
Iye anali ndi Davide ku Pasi-Damimu pamene Afilisti anasonkhana kudzachita nkhondo. Ankhondo anathawa Afilistiwo pamalo pamene panali munda wodzaza ndi barele.
14 And he took his stand in the midst of the plot, and defended it, and killed the Philistines; and YHWH saved them by a great victory.
Koma awiriwo anayima pakati pa mundawo. Iwo anawuteteza, nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
15 And three of the Thirty chief men went down to the rock to David, into the cave of Adullam; and the army of the Philistines were camped in the Valley of Rephaim.
Atatu mwa atsogoleri makumi atatu aja anabwera kwa Davide ku thanthwe ku phanga la Adulamu pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
16 David was then in the stronghold, and the garrison of the Philistines was then in Bethlehem.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
17 And David had a craving and said, "Oh that one would give me water to drink of the well of Bethlehem, which is by the gate."
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
18 The Three broke through the army of the Philistines, and drew water out of the well of Bethlehem, that was by the gate, and took it, and brought it to David: but David would not drink of it, but poured it out to YHWH,
Choncho anthu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
19 and said, "My God forbid it me, that I should do this. Shall I drink the blood of these men who have put their lives in jeopardy?" For they risked their lives to bring it. Therefore he would not drink it. The Three warriors did these things.
Iye anati, “Inu Mulungu, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi ndimwe magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Chifukwa iwo anayika miyoyo yawo pachiswe kuti abweretse madziwo, Davide sanamwe. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
20 And Abishai, the brother of Joab, was leader of the Thirty. And he wielded his spear against three hundred and killed them, and had a name beside the Three.
Abisai mʼbale wa Yowabu ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300. Choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
21 He was the most illustrious of the Thirty, and he became their leader. However, he did not attain to the Three.
Iye analandira ulemu woposa atatuwo. Kotero anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti iyeyo sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
22 Benaiah the son of Jehoiada was a valiant man of Kabzeel, who performed great deeds. He killed the two of Ariel of Moab. He also went down and killed a lion in the midst of a pit in time of snow.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
23 He killed an Egyptian, a man of great stature, seven feet five inches tall; and in the Egyptian's hand was a spear like a weaver's beam; and he went down to him with a staff, and grabbed the spear out of the Egyptian's hand, and killed him with his own spear.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto amene anali wotalika mamita awiri ndi theka. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo wofanana ndi ndodo yowombera nsalu mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
24 Benaiah the son of Jehoiada did these things, and had a name among the Three warriors.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
25 Look, he was more honored than the Thirty, but he did not attain to the Three. And David set him over his guard.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
26 Also the warriors of the armies: Asahel the brother of Joab, Elhanan the son of Dodo of Bethlehem,
Ankhondo amphamvuwa anali: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
27 Shammah the Harodite, Elika the Harodite, Helez the Paltite,
Samoti Mharori, Helezi Mpeloni.
28 Ira the son of Ikkesh the Tekoite, Abiezer the Anathothite,
Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa, Abiezeri wa ku Anatoti,
29 Sibbekai the Hushathite, Zalmon the Ahohite,
Sibekai Mhusati, Ilai Mwahohi,
30 Maharai the Netophathite, Heled the son of Baanah the Netophathite,
Maharai Mnetofa, Heledi mwana wa Baana Mnetofa,
31 Ithai the son of Ribai of Gibeah of the people of Benjamin, Benaiah the Pirathonite,
Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini, Benaya Mpiratoni,
32 Hiddai of Nahale Gaash, Abiel the Arbathite,
Hurai wa ku zigwa za Gaasi, Abieli Mwaribati,
33 Azmaveth the Bahurimite, Eliahba the Shaalbinite,
Azimaveti Mbaharumi, Eliyahiba Msaaliboni,
34 Jashen the Gizonite, Jonathan the son of Shamma the Hararite,
ana a Hasemu Mgizoni, Yonatani mwana wa Sage Mharari,
35 Ahiam the son of Sakar the Hararite, Eliphelet the son of Ahasbai the Maacathite,
Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,
36 Eliam the son of Ahithophel the Gilonite,
Heferi Mmekerati, Ahiya Mpeloni,
37 Hezrai the Carmelite, Paarai the Archite,
Heziro wa ku Karimeli Naara mwana wa Ezibai,
38 Igal the son of Nathan, from the elite troops of the Hagrites,
Yoweli mʼbale wa Natani, Mibihari mwana wa Hagiri,
39 Zelek the Ammonite, Naharai the Beerothite, the armor bearer of Joab the son of Zeruiah,
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya.
40 Ira the Jattirite, Gareb the Jattirite,
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
41 Uriah the Hethite, Zabad the son of Ahlai,
Uriya Mhiti, Zabadi mwana wa Ahilai,
42 Adina the son of Shiza the Reubenite, a chief of the Reubenites, and thirty with him,
Adina mwana wa Siza Mrubeni, amene anali mtsogoleri wa Arubeni ndi anthu makumi atatu pamodzi naye,
43 Hanan the son of Maacah, and Joshaphat the Mithnite,
Hanani mwana wa Maaka, Yehosafati Mmitini,
44 Uzzia the Ashterathite, Shama and Jeiel the sons of Hotham the Aroerite,
Uziya Mwasiterati, Sama ndi Yeiyeli ana a Hotamu Mwaroeri,
45 Jediael the son of Shimri, and Joha his brother, the Tizite,
Yediaeli mwana wa Simiri, ndi Yoha Mtizi mʼbale wake,
46 Eliel the Mahavite, and Jeribai, and Joshaviah, the sons of Elnaam, and Ithmah the Moabite,
Elieli Mhavati, Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, Itima Mmowabu,
47 Eliel, and Obed, and Jaasiel the Mezobaiah.
Elieli, Obedi ndi Yaasieli Mmeobai.