< Isaiah 12 >
1 In that day you will say, "I will give thanks to you, the LORD; for you were angry with me, but your anger has turned away and you comfort me.
Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
2 Look, in the God of my salvation I will trust, and will not be afraid. For the LORD is my strength and my song, and he has become my salvation."
Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 Therefore with joy you will draw water out of the wells of salvation.
Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 In that day you will say, "Give thanks to the LORD. Call on his name. Declare his doings among the peoples. Proclaim that his name is exalted.
Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Sing to the LORD, for he has done excellent things. Let this be known in all the earth.
Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Cry aloud and shout, you inhabitant of Zion; for the Holy One of Israel is great in the midst of you."
Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”