< Genesis 9 >

1 God blessed Noah and his sons, and said to them, "Be fruitful, and multiply, and fill the earth.
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
2 And the fear of you and the dread of you will be on every wild animal of the earth, and on every tame animal of the earth, and on every flying creature of the sky, and on everything that crawls on the ground, and on all the fish of the sea; into your power they are given.
Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
3 Every moving thing that lives will be food for you. As I gave the green plants, I now give you everything.
Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
4 But flesh with its life, its blood, you shall not eat.
“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
5 And surely I will require a reckoning for your lifeblood; from every animal I will require it, and from humans. From every human being I will require it for the life of his fellow human being.
Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
6 Whoever takes a human life, by a human will his life be taken, for God made humankind in his own image.
“Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
7 And as for you, be fruitful and multiply, and increase abundantly on the earth, and subdue it."
Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
8 God spoke to Noah and to his sons with him, saying,
Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
9 "And as for me, look, I establish my covenant with you, and with your offspring after you,
“Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
10 and with every living creature that is with you: the flying creatures, and the tame animals, and every wild animal of the earth with you, of all that go out of the ship.
pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
11 I will establish my covenant with you; and all flesh will never again be cut off by the waters of the flood, neither will there ever again be a flood to destroy the earth."
Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
12 God said, "This is the sign of the covenant which I make between me and you and every living creature that is with you, for perpetual generations:
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
13 I set my rainbow in the cloud, and it will be a sign of the covenant between me and the earth.
Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
14 It will happen, when I bring a cloud over the earth, that the rainbow will be seen in the cloud,
Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
15 and I will remember my covenant, which is between me and you and every living creature of all flesh, and the waters will no more become a flood to destroy all flesh.
ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
16 The rainbow will be in the cloud. I will look at it, that I may remember the everlasting covenant between me and every living creature of all flesh that is on the earth."
Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
17 God said to Noah, "This is the sign of the covenant which I have established between me and all flesh that is on the earth."
Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
18 The sons of Noah who came out of the ship were Shem, Ham, and Japheth. Ham is the father of Canaan.
Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
19 These were the three sons of Noah, and from them the whole earth was populated.
Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
20 Noah, a farmer, was the first to plant a vineyard.
Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
21 He drank of the wine and got drunk. He was uncovered within his tent.
Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
22 And Ham, the father of Canaan, saw his father naked and told his two brothers outside.
Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
23 Shem and Japheth took a garment, and laid it on both their shoulders, went in backwards, and covered the nakedness of their father. Their faces were turned the other way, and they did not see their father's nakedness.
Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
24 Noah awoke from his wine, and knew what his youngest son had done to him.
Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
25 He said, "Canaan is cursed. He will be servant of servants to his brothers."
anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
26 He said, "Blessed be the God of Shem. Let Canaan be his servant.
Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
27 May God enlarge Japheth. Let him dwell in the tents of Shem. Let Canaan be his servant."
Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
28 Noah lived three hundred fifty years after the flood.
Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
29 All the days of Noah were nine hundred and fifty years, then he died.
Anamwalira ali ndi zaka 950.

< Genesis 9 >