< Zechariah 1 >

1 In the eighth month, in the second year of Daryavesh, the word of the LORD came to Zechariah the son of Berechiah, the son of Iddo, the prophet, saying,
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2 "The LORD was very displeased with your fathers.
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
3 Therefore tell them: Thus says the LORD of hosts: 'Return to me,' says the LORD of hosts, 'and I will return to you,' says the LORD of hosts.
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Do not be like your fathers, to whom the former prophets proclaimed, saying: Thus says the LORD of hosts, 'Return now from your evil ways, and from your evil doings;' but they did not hear, nor listen to me, says the LORD.
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
5 Your fathers, where are they? And the prophets, do they live forever?
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
6 But my words and my statutes, which I commanded by my Ruach to my servants the prophets, did they not overtake your fathers? Then they repented and said, 'Just as the LORD of hosts determined to do to us, according to our ways, and according to our practices, so he has dealt with us.'"
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
7 On the twenty-fourth day of the eleventh month, which is the month Shebat, in the second year of Daryavesh, the word of the LORD came to Zechariah the son of Berechiah, the son of Iddo, the prophet, saying,
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8 "I had a vision in the night, and look, a man riding on a red horse, and he stood among the myrtle trees that were in a ravine; and behind him there were red, brown, and white horses.
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9 Then I asked, 'My lord, what are these?'" The angel who talked with me said to me, "I will show you what these are."
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10 The man who stood among the myrtle trees answered and said to me, "They are the ones the LORD has sent to go back and forth through the earth."
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11 They reported to the angel of the LORD who stood among the myrtle trees, and said, "We have walked back and forth through the earth, and look, all the earth is at rest and in peace."
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12 Then the angel of the LORD replied, "O LORD of hosts, how long will you not have mercy on Jerusalem and on the cities of Judah, against which you have had indignation these seventy years?"
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
13 The LORD answered the angel who talked with me with kind and comforting words.
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14 So the angel who talked with me said to me, "Proclaim, saying, 'Thus says the LORD of hosts: "I am jealous for Jerusalem and for Zion with a great jealousy.
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
15 I am very angry with the nations that are at ease; for I was but only a little angry, but they added to the calamity."
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16 Therefore thus says the LORD: "I have returned to Jerusalem with mercy. My house will be built in it," says the LORD of hosts, "and a line shall be stretched forth over Jerusalem."'
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17 "Proclaim further, saying, 'Thus says the LORD of hosts: "My cities will again overflow with prosperity, and the LORD will again comfort Zion, and will again choose Jerusalem."'"
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
18 I lifted up my eyes, and saw, and look, four horns.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
19 I asked the angel who talked with me, "What are these?" He answered me, "These are the horns which have scattered Judah, Israel, and Jerusalem."
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20 The LORD showed me four craftsmen.
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
21 Then I asked, "What are these coming to do?" He said, "These are the horns which scattered Judah, so that no man lifted up his head; but these have come to terrify them, to cast down the horns of the nations, which lifted up their horn against the land of Judah to scatter it."
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”

< Zechariah 1 >