< Psalms 105 >

1 Give thanks to the LORD. Call on his name. Make his deeds known among the peoples.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Sing to him, sing praises to him. Tell of all his marvelous works.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Glory in his holy name. Let the heart of those who seek the LORD rejoice.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Seek the LORD and his strength. Seek his face forever more.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Remember his marvelous works that he has done; his wonders, and the judgments of his mouth,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 you offspring of Abraham, his servant, you descendants of Jacob, his chosen ones.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 He is the LORD, our God. His judgments are in all the earth.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 He has remembered his covenant forever, the word which he commanded to a thousand generations,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 the covenant which he made with Abraham, his oath to Isaac,
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 and confirmed the same to Jacob for a statute; to Israel for an everlasting covenant,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 saying, "To you I will give the land of Canaan, the lot of your inheritance;"
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 when they were but a few men in number, yes, very few, and foreigners in it.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 They went about from nation to nation, from one kingdom to another people.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 He allowed no one to do them wrong. Yes, he reproved kings for their sakes,
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 "Do not touch my anointed ones. Do my prophets no harm."
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 He called for a famine on the land. He destroyed the food supplies.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 He sent a man ahead of them, Joseph, sold as a slave.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 They bruised his feet with shackles. His neck was locked in irons,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 until the time that his word happened, and the LORD's word proved him true.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 The king sent and freed him; even the ruler of peoples, and let him go free.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 He made him lord of his house, and ruler of all of his possessions;
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 to discipline his princes at his pleasure, and to teach his elders wisdom.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Israel also came into Egypt. Jacob sojourned in the land of Ham.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 He increased his people greatly, and made them stronger than their adversaries.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 He turned their heart to hate his people, to conspire against his servants.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 He sent Moses, his servant, and Aaron, whom he had chosen.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 They performed miracles among them, and wonders in the land of Ham.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 He sent darkness, and made it dark, but they rebelled against his words.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 He turned their waters into blood, and killed their fish.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Their land swarmed with frogs, even in the chambers of their kings.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 He spoke, and swarms of flies came, and gnats in all their territory.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 He gave them hail for rain, flaming fire in their land.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 He struck their vines and also their fig trees, and shattered the trees of their country.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 He spoke, and the locusts came, and the grasshoppers, without number,
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 ate up every plant in their land; and ate up the fruit of their ground.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 He struck also all the firstborn in their land, the first fruits of all their manhood.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 And he brought them out with silver and gold, and there was no one among their tribes who stumbled.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Egypt was glad when they departed, for the fear of them had fallen on them.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 He spread a cloud for a covering, fire to give light in the night.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 They asked, and he brought quails, and satisfied them with the bread of the sky.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 He opened the rock, and waters gushed out. They ran as a river in the dry places.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 For he remembered his holy word, and Abraham, his servant.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 He brought forth his people with joy, his chosen with singing.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 He gave them the lands of the nations. They took the labor of the peoples in possession,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 that they might keep his statutes, and observe his laws. Praise the LORD.
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 105 >