< Joshua 17 >

1 This was the lot for the tribe of Manasseh, for he was the firstborn of Joseph. As for Makir the firstborn of Manasseh, the father of Gilead, because he was a man of war, therefore he had Gilead and Bashan.
Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
2 So this was for the rest of the descendants of Manasseh according to their families: for the descendants of Abiezer, for the descendants of Helek, for the descendants of Asriel, for the descendants of Shechem, for the descendants of Hepher, and for the descendants of Shemida: these were the male descendants of Manasseh the son of Joseph according to their families.
Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
3 But Zelophehad, the son of Hepher, the son of Gilead, the son of Makir, the son of Manasseh, had no sons, but daughters: and these are the names of his daughters: Mahlah, Noah, Hoglah, Milcah, and Tirzah.
Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
4 They came near before Eleazar the cohen, and before Joshua the son of Nun, and before the leaders, saying, "The LORD commanded Moses to give us an inheritance among our brothers." Therefore according to the commandment of the LORD he gave them an inheritance among the brothers of their father.
Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
5 Ten parts fell to Manasseh, besides the land of Gilead and Bashan, which is beyond the Jordan;
Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
6 because the daughters of Manasseh had an inheritance among his sons. The land of Gilead belonged to the rest of the sons of Manasseh.
chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
7 The border of Manasseh was from Asher to Michmethath, which is before Shechem. The border went along to the right hand to Jashub and to En Tappuah.
Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
8 The land of Tappuah belonged to Manasseh; but Tappuah, on the border of Manasseh, belonged to the descendants of Ephraim.
(Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
9 The border went down to Wadi Kanah, southward of the wadi. These cities belonged to Ephraim among the cities of Manasseh. The border of Manasseh was on the north side of the wadi, and ended at the sea.
Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
10 Southward it was Ephraim's, and northward it was Manasseh's, and the sea was his border. They reached to Asher on the north, and to Issachar on the east.
Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
11 And Manasseh had in Issachar and in Asher, Beth Shean and its towns, and Ibleam and its towns, and the inhabitants of Dor and its towns, and the inhabitants of Endor and its towns, and the inhabitants of Taanach and its towns, and the inhabitants of Megiddo and its towns; three regions.
Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
12 Yet the descendants of Manasseh couldn't drive out the inhabitants of those cities; but the Canaanites would dwell in that land.
Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
13 It happened, when the children of Israel had grown strong, that they put the Canaanites to forced labor, and did not utterly drive them out.
Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
14 The descendants of Joseph spoke to Joshua, saying, "Why have you given me just one lot and one part for an inheritance, since I am a great people, because the LORD has blessed me so far?"
Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
15 Joshua said to them, "If you are a great people, go up to the forest, and clear land for yourself there in the land of the Perizzites and of the Rephaim; since the hill country of Ephraim is too narrow for you."
Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
16 The descendants of Joseph said, "The hill country is not enough for us. All the Canaanites who dwell in the land of the valley have chariots of iron, both those who are in Beth Shean and its towns, and those who are in the Valley of Jezreel."
Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
17 Joshua spoke to the house of Joseph, even to Ephraim and to Manasseh, saying, "You are a great people, and have great power. You shall not have one lot only;
Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
18 but the hill country shall be yours. Although it is a forest, you shall cut it down, and its farthest extent shall be yours; for you shall drive out the Canaanites, though they have chariots of iron, and though they are strong."
dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”

< Joshua 17 >