< Genesis 30 >
1 When Rachel saw that she was not bearing Jacob any children, Rachel envied her sister. She said to Jacob, "Give me children, or else I will die."
Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
2 Then Jacob became very angry with Rachel, and he said, "Am I in God's place, who has withheld from you the fruit of the womb?"
Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
3 She said, "Look, my servant Bilhah. Sleep with her, so that she will bear children for me, that I too may have children through her."
Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
4 So she gave him Bilhah her servant as a wife, and Jacob slept with her.
Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
5 Bilhah conceived, and bore Jacob a son.
ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
6 Rachel said, "God has judged me, and has also heard my voice, and has given me a son." Therefore she called his name Dan.
Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
7 Bilhah, Rachel's handmaid, conceived again, and bore Jacob a second son.
Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
8 Rachel said, "I have wrestled mightily with my sister, and have prevailed." So she named him Naphtali.
Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
9 When Leah saw that she had stopped bearing, she took Zilpah, her servant, and gave her to Jacob as a wife.
Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
10 Zilpah, Leah's handmaid, bore Jacob a son.
Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
11 Leah said, "How fortunate." So she named him Gad.
Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
12 Zilpah, Leah's servant, bore Jacob a second son.
Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
13 Leah said, "Happy am I, for the women will call me happy." So she named him Asher.
Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
14 Reuben went out during the wheat harvest and found mandrakes in the field, and brought them to his mother, Leah. Then Rachel said to Leah, "Please give me some of your son's mandrakes."
Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
15 She said to her, "Is it a small matter that you have taken away my husband? Would you take away my son's mandrakes, also?" Rachel said, "Therefore he may sleep with you tonight for your son's mandrakes."
Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
16 Jacob came from the field in the evening, and Leah went out to meet him, and said, "You must sleep with me; for I have surely hired you with my son's mandrakes." So he slept with her that night.
Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
17 God listened to Leah, and she conceived, and bore Jacob a fifth son.
Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
18 Leah said, "God has given me my wages, because I gave my servant to my husband." So she named him Issachar.
Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
19 Leah conceived again, and bore a sixth son to Jacob.
Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
20 Leah said, "God has given me a good gift. Now my husband will live with me, because I have borne him six sons." So she named him Zebulun.
Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
21 Afterwards, she bore a daughter, and named her Dinah.
Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
22 God remembered Rachel, and God listened to her, and made her fertile.
Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
23 She conceived, bore a son, and said, "God has taken away my shame."
Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
24 So she named him Joseph, saying, "May God add another son to me."
Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
25 It happened, when Rachel had borne Joseph, that Jacob said to Laban, "Send me away, that I may go to my own place, and to my country.
Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
26 Give me my wives and my children for whom I have served you, and let me go; for you know the service I have given you."
Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
27 Laban said to him, "If now I have found favor in your eyes, stay here, for I have learned by divination that God has blessed me for your sake."
Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
28 He said, "Name your wages, and I will pay it."
Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
29 He said to him, "You know how I have served you, and how well your livestock have done with me.
Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
30 For you had little before I came, and it has increased abundantly. And God has blessed you wherever I worked. Now when will I also provide for my own household?"
Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
31 He said, "What should I give you?" Jacob said, "You do not need to give me anything. If you will do this one thing for me, I will again pasture your flock and take care of it.
Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
32 I will pass through all your flock today, removing from there every speckled and spotted one, and every black one among the sheep, and the spotted and speckled among the goats. This will be my wages.
Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
33 So my honesty will testify for me later on, when the subject of my wages comes before you. Every one that is not speckled and spotted among the goats, and black among the sheep that I have in my possession, will be counted as stolen."
Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
34 Laban said, "Look, let it be as you have said."
Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
35 That day, he removed the male goats that were streaked and spotted, and all the female goats that were speckled and spotted, every one that had white in it, and all the black ones among the sheep, and put them in the care of his sons.
Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
36 He set three days' journey between himself and Jacob, and Jacob pastured the rest of Laban's flocks.
Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
37 Jacob took fresh branches from poplar, almond and plane trees and made white streaks by peeling them, exposing white stripes on the branches.
Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
38 He set up the peeled branches which he had peeled opposite the flocks in the troughs, that is, the watering places where the flocks came to drink. And since they bred when they came to drink,
Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
39 the flocks bred in front of the branches, and the flocks brought bore streaked, speckled, and spotted.
Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
40 Jacob separated the lambs, and made the flocks face toward the streaked and all the black in the flock of Laban. So he kept his own flocks separate, and did not put them into Laban's flock.
Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
41 It happened, whenever the stronger of the flock were breeding, that Jacob would set up the branches in front of the flock in the troughs, so that they would breed near the branches;
Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
42 but for the weaker of the flock, he did not put them there. So the weaker would be Laban's, and the stronger Jacob's.
Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
43 Thus the man became very rich, and had large flocks, female servants and male servants, and camels and donkeys.
Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.