< Genesis 2 >

1 Thus the heavens and the earth were finished, and all their vast array.
Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.
2 And on the sixth day God finished his works which he had made; and he rested on the seventh day from all his works which he had made.
Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse.
3 So God blessed the seventh day, and made it holy, because he rested on it from all his works which God had created and made.
Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
4 This is the account of the heavens and of the earth when they were created, at the time when God made the earth and the heavens.
Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,
5 Now no bush of the field was yet in the land, and no plant of the field had yet sprouted; for God had not caused it to rain on the land, and there were no people to cultivate the ground,
zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka,
6 but springs came up from the earth and watered the whole surface of the ground.
koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse.
7 And God formed man from the dust of the ground, and breathed into his nostrils the breath of life; and man became a living being.
Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
8 And God planted a garden eastward, in Eden, and there he put the man whom he had formed.
Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja.
9 And out of the ground God made every tree to grow that is pleasant to the sight, and good for food; the tree of life also in the middle of the garden, and the tree of the knowledge of good and evil.
Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.
10 And a river went out of Eden to water the garden; and from there it separated and became the source of four rivers.
Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi.
11 The name of the first is Pishon; this is the one which goes around the whole land of Havilah, where there is gold;
Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide.
12 and the gold of that land is good. There is aromatic resin and the onyx stone.
(Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi).
13 And the name of the second river is Gihon; it goes around the whole land of Cush.
Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi.
14 And the name of the third river is Hiddekel; this is the one which flows east of Ashur. And the fourth river is the Perath.
Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.
15 And God took the man, and put him into the garden of Eden to cultivate it and take care of it.
Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira.
16 And God commanded the man, saying, "Of every tree of the garden you may freely eat;
Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu;
17 but of the tree of the knowledge of good and evil, you shall not eat of it; for in the day that you eat of it you will surely die."
koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”
18 And God said, "It is not good that the man should be alone; I will make him a helper suitable for him."
Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
19 And out of the ground God formed every tame animal, and every wild animal, and every flying creature of the sky, and brought them to the man to see what he would call them. And whatever the man called each living creature, that was its name.
Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake.
20 And the man gave names to all the tame animals, and to all the flying creatures of the sky, and to every wild animal; but for Adam there was not found a helper suitable for him.
Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse. Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza.
21 So God caused a deep sleep to fall on the man, and he slept; and he took one of his ribs, and closed up the flesh at that place.
Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu.
22 And the rib that God had taken from the man he fashioned into a woman and brought her to the man.
Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.
23 And the man said, "This at last is bone of my bones, and flesh of my flesh. She will be called Woman, because this one was taken out of Man."
Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
24 Therefore a man will leave his father and his mother, and will join with his wife, and the two will become one flesh.
Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
25 And They were both naked, the man and his wife, and were not ashamed.
Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.

< Genesis 2 >