< Ephesians 4 >

1 I therefore, a prisoner in the Lord, urge you to lead a life worthy of the calling to which you have been called,
Ine monga wamʼndende chifukwa chotumikira Ambuye, ndikukulimbikitsani kuti mukhale moyo woyenera mayitanidwe amene munalandira.
2 with all humility and gentleness, with patience, bearing with one another in love;
Mukhale odzichepetsa kwathunthu ndi ofatsa; mukhale oleza mtima, ololerana wina ndi mnzake mwachikondi.
3 being eager to keep the unity of the Ruach in the bond of peace.
Muyesetse kusunga umodzi wa Mzimu; umodzi umene umatimangirira pamodzi mu mtendere.
4 There is one body, and one Ruach, even as you also were called in one hope of your calling;
Pali thupi limodzi ndiponso Mzimu mmodzi, monganso pali chiyembekezo chimodzi chimene anakuyitanirani.
5 one Lord, one faith, one immersion,
Pali Ambuye mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi;
6 one God and Father of all, who is over all, and through all, and in all.
Mulungu mmodzi ndi Atate a onse, ndipo ali mwa onse.
7 But to each one of us was the grace given according to the measure of the gift of Messiah.
Koma aliyense wa ife wapatsidwa chisomo molingana ndi muyeso wa mphatso ya Khristu.
8 Therefore he says, "When he ascended on high, he led captivity captive, and gave gifts to people."
Nʼchifukwa chake akunena kuti, “Iye atakwera kumwamba, anatenga chigulu cha a mʼndende ndipo anapereka mphatso kwa anthu.”
9 Now this, "He ascended," what is it but that he also descended into the lower parts of the earth?
Kodi mawu akuti, “Iye anakwera” akutanthauza chiyani, ngati Iyeyo sanatsikire kunsi kwa dziko lapansi?
10 He who descended is the one who also ascended far above all the heavens, that he might fill all things.
Iye amene anatsika ndi yemweyo anakwera koposa mʼmayiko a kumwamba onse, ndi cholinga choti zinthu zonse zikhale zodzaza ndi Iye.
11 He gave some to be emissaries; and some, prophets; and some, evangelists; and some, pastors and teachers;
Iye ndiye amene anapereka mphatso kwa ena kuti akhale atumwi ndi ena aneneri, ena alaliki, ndi ena abusa ndi aphunzitsi.
12 for the perfecting of the kadoshim, to the work of serving, to the building up of the body of Messiah;
Ntchito yawo ndi kukonza oyera mtima kuti agwire ntchito ya utumiki kuti thupi la Khristu lilimbikitsidwe.
13 until we all attain to the unity of the faith, and of the knowledge of the Son of God, to a mature person, to the measure of the stature of the fullness of Messiah;
Izi zidzatifikitsa tonse ku umodzi wachikhulupiriro, kumudziwa Mwana wa Mulungu, kukhwima msinkhu ndi kufika pa muyeso wangwiro weniweni wopezeka mwa Khristu.
14 that we may no longer be children, tossed back and forth and carried about with every wind of doctrine, by the trickery of people, by cleverness in deceitful schemes;
Motero sitidzakhalanso makanda, ogwedezekagwedezeka ndi mafunde, otengekatengeka ndi mphepo iliyonse ya chiphunzitso ndi kuchenjera kwa anthu achinyengo amene amasocheretsa anthu ndi kuchenjera kwawo.
15 but speaking truth in love, we may grow up in all things into him, who is the head, Messiah;
Mʼmalo mwake, poyankhula choonadi mwachikondi, tidzakula mu zinthu zonse ndi kukhala thupi la Khristu, amene ndi Mutu, omwe ndi mpingo.
16 from whom all the body, being fitted and knit together through that which every joint supplies, according to the proper working of each individual part, makes the body increase to the building up of itself in love.
Mwa Iye thupi lonse lalumikizidwa ndi kugwirana pamodzi ndi mitsempha yothandizira. Likukula ndi kudzilimbitsa lokha mwachikondi, pomwe chiwalo chilichonse chikugwira ntchito yake.
17 This I say therefore, and testify in the Lord, that you no longer walk as the nations also walk, in the futility of their mind,
Tsono ine ndikukuwuzani izi, ndipo ndikunenetsa mwa Ambuye, kuti musayendenso monga amachitira anthu a mitundu ina potsata maganizo awo opanda pake.
18 being darkened in their understanding, alienated from the life of God, because of the ignorance that is in them, because of the hardening of their hearts;
Maganizo awo ndi odetsedwa, ndi osiyanitsidwa ndi moyo wa Mulungu chifukwa cha umbuli umene uli mwa iwo chifukwa cha kuwuma mtima kwawo.
19 who having become callous gave themselves up to lust, to work all uncleanness with greediness.
Popeza sazindikiranso kanthu kalikonse, adzipereka okha kuti akhumbe zonyansa, kuti achite mtundu uliwonse wa zoyipa ndi zilakolako zosatha.
20 But you did not learn Messiah that way;
Koma inu simunadziwe Khristu mʼnjira yotere.
21 if indeed you heard him, and were taught in him, even as truth is in Yeshua:
Zoonadi munamva za Iye ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye molingana ndi choonadi chimene chili mwa Yesu.
22 that you put away, as concerning your former way of life, the old self, that grows corrupt after the lusts of deceit;
Inu munaphunzitsidwa molingana ndi moyo wanu wakale, kuchotsa umunthu wakale, umene ukupitirira kuwonongeka ndi zilakolako zachinyengo;
23 and that you be renewed in the spirit of your mind,
kuti mukonzedwe mwatsopano mʼmitima mwanu;
24 and put on the new self, who in the likeness of God has been created in righteousness and holiness of truth.
ndi kuti muvale umunthu watsopano, wolengedwa kuti ufanane ndi Mulungu mu chilungamo chenicheni ndi chiyero.
25 Therefore, putting away falsehood, speak truth each one with his neighbor. For we are members of one another.
Chifukwa chake, aliyense wa inu aleke kunama ndipo ayankhule zoona kwa mʼbale wake, pakuti ife tonse ndife ziwalo za thupi limodzi.
26 "Be angry, but do not sin." Do not let the sun go down on your anger,
Kwiyani koma musachimwe. Dzuwa lisalowe mukanali chikwiyire.
27 neither give place to the devil.
Musamupatse mpata Satana.
28 Let him who stole steal no more; but rather let him labor, working with his hands the thing that is good, that he may have something to give to him who has need.
Iye amene wakhala akuba asabenso, koma agwire ntchito ndi kuchita kenakake kaphindu ndi manja ake, kuti akhale ndi kenakake kogawana ndi amene akusowa.
29 Let no corrupt speech proceed out of your mouth, but such as is good for building up as the need may be, that it may give grace to those who hear.
Mʼkamwa mwanu musatuluke mawu aliwonse onyansa, koma okhawo amene ndi othandiza kulimbikitsa ena molingana ndi zosowa zawo, kuti athandize amene akawamve.
30 Do not grieve the Ruach ha-Kodesh of God, in whom you were sealed for the day of redemption.
Ndipo musamvetse chisoni Mzimu Woyera wa Mulungu amene mwasindikizidwa naye chizindikiro cha tsiku la kuwomboledwa.
31 Let all bitterness, wrath, anger, outcry, and slander, be put away from you, with all malice.
Chotsani kuzondana, ukali ndi kupsa mtima, chiwawa ndi kuyankhula zachipongwe, pamodzi ndi choyipa chilichonse.
32 And be kind to one another, tenderhearted, forgiving each other, just as God also in Messiah forgave you.
Mukomerane mtima ndi kuchitirana chifundo wina ndi mnzake. Khululukiranani wina ndi mnzake, monga momwe Mulungu anakukhululukirani mwa Khristu.

< Ephesians 4 >