< 2 Samuel 11 >

1 It happened, at the return of the year, at the time when kings go out, that David sent Joab, and his servants with him, and all Israel; and they destroyed the people of Ammon, and besieged Rabbah. But David stayed at Jerusalem.
Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
2 Now it happened one evening that David got up from his bed and walked on the roof of the king's palace; and he saw a woman bathing, and the woman was very beautiful.
Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
3 And David sent and inquired about the woman. And one said, "Isn't this Bathsheba, the daughter of Eliam, the wife of Uriah the Hethite?"
Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
4 So David sent messengers to get her, and she came in to him, and he lay with her. (For she had been purifying herself from her uncleanness.) And she returned to her house.
Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
5 The woman conceived; and she sent and told David, and said, "I'm pregnant."
Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
6 Then David sent to Joab and said, "Send me Uriah the Hethite." So Joab sent Uriah to him.
Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
7 And Uriah came to him, and David asked about the prosperity of Joab, and of the prosperity of the people, and of the prosperity of the war. And he said, "Its well."
Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
8 And David said to Uriah, "Go down to your house, and wash your feet." So Uriah went out from the presence of the king, and a gift from the king was sent after him.
Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
9 But Uriah slept at the king's door with his master's servants, and did not go down to his house.
Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
10 And it was reported to David, saying, "Uriah did not go down to his house." So David said to Uriah, "Haven't you come from a journey? Why did you not go down to your house?"
Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
11 And Uriah said to David, "The ark and Israel and Judah are staying in tents; and my lord Joab and the servants of my lord are camped in the open field. Then how can I go to my house to eat and to drink and to lie with my wife? As the LORD lives, and as you live, I will not do this thing."
Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
12 David said to Uriah, "Stay here today also, and tomorrow I will let you depart." So Uriah stayed in Jerusalem that day.
Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
13 And the next day David summoned him, and he ate and drank in his presence, and he became drunk. But in the evening he went out and lay on a bed with his master's servants, and did not go down to his house.
Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
14 It happened in the morning, that David wrote a letter to Joab, and sent it by the hand of Uriah.
Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
15 He wrote in the letter, saying, "Send Uriah to the forefront of the hottest battle, and retreat from him, that he may be struck down and die."
Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
16 It happened, when Joab kept watch on the city, that he assigned Uriah to the place where he knew that valiant men were.
Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
17 The men of the city went out, and fought with Joab. Some of the people fell, even of the servants of David; and Uriah the Hethite died also.
Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
18 Then Joab sent and told David all the things concerning the war;
Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
19 and he commanded the messenger, saying, "When you have finished telling all the things concerning the war to the king,
Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
20 if it happens that he becomes angry,
mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
21 then you are to say, 'Your servant Uriah the Hethite is dead also.'"
Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
22 So the messenger of Joab went to the king in Jerusalem and reported to David everything that Joab had told him.
Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
23 The messenger said to David, "The men overpowered us, and came out to us into the field, and when we drove them back to the entrance of the gate,
Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
24 then the arrows came down heavily on your servants from the wall, and some eighteen men of the king's servants died." And the messenger finished the words to the king about the report of the battle. Then David was very angry with Joab, and said to the messenger, "Why did you go so close to the city to fight? Didn't you know you would be struck from the wall? Who struck Abimelech the son of Jerubbaal? Didn't a woman cast an upper millstone on him from the wall so that he died at Thebez? Why did you go so near to the wall?" [Then he said to the king, ] "Also your servant Uriah the Hethite is dead."
Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
25 Then David said to the messenger, "Thus you shall tell Joab, 'Do not let this thing displease you, for the sword devours one as well as another. Make your battle stronger against the city, and overthrow it.' And encourage him."
Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
26 When the wife of Uriah heard that Uriah her husband was dead, she made lamentation for her husband.
Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
27 When the mourning was past, David sent and took her home to his house, and she became his wife, and bore him a son. But the thing that David had done displeased the LORD.
Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.

< 2 Samuel 11 >