< 1 Samuel 24 >

1 It happened, when Saul was returned from following the Philistines, that it was told him, saying, "Look, David is in the wilderness of En Gedi."
Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
2 Then Saul took three thousand chosen men out of all Israel, and went to seek David and his men on the rocks of the wild goats.
Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
3 He came to the sheep pens by the way, where there was a cave; and Saul went in to relieve himself. Now David and his men were abiding in the innermost parts of the cave.
Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
4 The men of David said to him, "Look, the day of which the LORD said to you, 'Look, I will deliver your enemy into your hand, and you shall do to him as it shall seem good to you.'" Then David arose, and cut off an edge of Saul's robe secretly.
Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
5 It happened afterward, that David's heart struck him, because he had cut off an edge of Saul's robe.
Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
6 He said to his men, "The LORD forbid that I should do this thing to my lord, the LORD's anointed, to put forth my hand against him, since he is the LORD's anointed."
Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
7 So David persuaded his men with these words and did not allow them to rise up against Saul. Then Saul got up, and went down the road.
Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
8 Afterward David also got up and left the cave, and called out after Saul, saying, "My lord the king." When Saul looked behind him, David bowed with his face to the ground and did homage.
Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
9 David said to Saul, "Why do you listen to men's words, saying, 'Look, David seeks your harm?'
Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
10 Look, this day your eyes have seen how that the LORD had delivered you today into my hand in the cave, but I refused to kill you, and my eye spared you; and I said, 'I will not put forth my hand against my lord; for he is the LORD's anointed.'
Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
11 Now look, the skirt of your robe in my hand. When I cut off the skirt, and did not kill you, know and see that there is neither evil nor disobedience in my hand, and I have not sinned against you, though you hunt for my life to take it.
Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
12 May the LORD judge between me and you, and may the LORD avenge me of you; but my hand shall not be on you.
Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
13 As the proverb of the ancients says, 'Out of the wicked comes forth wickedness;' but my hand shall not be on you.
Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
14 Against whom has the king of Israel come out? Whom do you pursue? After a dead dog, or one flea?
“Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
15 May the LORD therefore be judge and give sentence between me and you. May he see and plead my cause, and deliver me out of your hand."
Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
16 It came to pass, when David had made an end of speaking these words to Saul, that Saul said, "Is this your voice, my son David?" Saul lifted up his voice, and wept.
Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
17 He said to David, "You are more righteous than I; for you have done good to me, whereas I have done evil to you.
Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
18 And you have declared this day how you have dealt well with me, in that the LORD had delivered me up into your hand and you did not kill me.
Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
19 For if a man finds his enemy, will he let him go away unharmed? Therefore may the LORD reward you good for that which you have done this day.
Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
20 Now, look, I know that you shall surely be king, and that the kingdom of Israel shall be established in your hand.
Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
21 Swear now therefore to me by the LORD, that you will not cut off my descendants after me, and that you will not destroy my name out of my father's house."
Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
22 David swore to Saul. Saul went home; but David and his men went up to the stronghold.
Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.

< 1 Samuel 24 >