< Deuteronomy 15 >

1 At the end of every seven years you shall make a release.
Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
2 This is the way of the release: every creditor shall release that which he has lent to his neighbor; he shall not exact it of his neighbor and his brother; because the LORD's release has been proclaimed.
Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
3 Of a foreigner you may exact it: but whatever of yours is with your brother your hand shall release.
Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
4 However there shall be no poor with you; (for the LORD will surely bless you in the land which the LORD your God gives you for an inheritance to possess it; )
Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
5 if only you diligently listen to the voice of the LORD your God, to observe to do all this commandment which I command you this day.
Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
6 For the LORD your God will bless you, as he promised you: and you shall lend to many nations, but you shall not borrow; and you shall rule over many nations, but they shall not rule over you.
Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
7 If a poor man, one of your brothers, is with you within any of your gates in your land which the LORD your God gives you, you shall not harden your heart, nor shut your hand from your poor brother;
Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
8 but you shall surely open your hand to him, and shall surely lend him sufficient for his need, which he lacks.
Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
9 Be careful lest there be a wicked thought in your heart, saying, "The seventh year, the year of release, is at hand"; and your eye be evil against your poor brother, and you give him nothing; and he cry to the LORD against you, and it be sin to you.
Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
10 You must surely give to him, and your heart is not to be grieved when you give to him; because for this thing the LORD your God will bless you in all your work, and in all that you put your hand to.
Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
11 For the poor will never cease out of the land: therefore I command you, saying, You shall surely open your hand to your brother, to your needy, and to your poor, in your land.
Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
12 If your brother, a Hebrew man, or a Hebrew woman, is sold to you, and serves you six years; then in the seventh year you shall let him go free from you.
Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
13 When you let him go free from you, you shall not let him go empty:
Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
14 you shall furnish him liberally out of your flock, and out of your threshing floor, and out of your winepress, in proportion as the LORD your God has blessed you, you shall give to him.
Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
15 You shall remember that you were a bondservant in the land of Egypt, and the LORD your God redeemed you: therefore I command you this thing today.
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
16 It shall be, if he tells you, "I will not go out from you"; because he loves you and your house, because he is well with you;
Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
17 then you shall take an awl, and thrust it through his ear to the door, and he shall be your servant forever. Also to your female servant you shall do likewise.
pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
18 It shall not seem hard to you, when you let him go free from you; for to the double of the hire of a hireling has he served you six years: and the LORD your God will bless you in all that you do.
Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
19 All the firstborn males that are born of your herd and of your flock you shall sanctify to the LORD your God: you shall do no work with the firstborn of your herd, nor shear the firstborn of your flock.
Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
20 You shall eat it before the LORD your God year by year in the place which the LORD shall choose, you and your household.
Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
21 If it has any blemish, is lame or blind, or has any defect whatever, you shall not sacrifice it to the LORD your God.
Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
22 You shall eat it within your gates: the unclean and the clean shall eat it alike, as the gazelle, and as the deer.
Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
23 Only you shall not eat its blood; you shall pour it out on the ground as water.
Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.

< Deuteronomy 15 >