< John 7 >
1 After these things, Jesus was walking in Galilee, for he would not walk in Judea, because the Jewish leaders sought to kill him.
Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
2 Now the Jewish festival, the Feast of Tabernacles, was near.
Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
3 So his brothers said to him, "Depart from here, and go into Judea, that your disciples also may see your works that you are doing.
abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
4 For no one does anything in secret when he himself seeks to be known openly. If you do these things, show yourself to the world."
Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
5 For even his brothers did not believe in him.
Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
6 Jesus therefore said to them, "My time has not yet come, but your time is always ready.
Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
7 The world cannot hate you, but it hates me, because I testify about it, that its works are evil.
Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
8 You go up to the feast. I am not yet going up to this feast, because my time is not yet fulfilled."
Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
9 After he had said this, he stayed in Galilee.
Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
10 But when his brothers had gone up to the feast, then he also went up, not publicly, but as it were in secret.
Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
11 The Jewish leaders therefore sought him at the feast, and said, "Where is he?"
Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
12 There was much murmuring among the crowds concerning him. Some said, "He is a good man." But others said, "Not so, but he leads the crowd astray."
Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
13 Yet no one spoke openly of him for fear of the Jewish leaders.
Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
14 But when it was now the midst of the feast, Jesus went up into the temple and taught.
Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
15 Then the Jewish leaders were astonished, saying, "How does this man know such writings, having never been educated?"
Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
16 Jesus therefore answered them, "My teaching is not mine, but his who sent me.
Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
17 If anyone desires to do his will, he will know about the teaching, whether it is from God, or if I am speaking from myself.
Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
18 He who speaks from himself seeks his own glory, but he who seeks the glory of him who sent him is true, and no unrighteousness is in him.
Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
19 Did not Moses give you the Law, and yet none of you keeps the Law? Why do you seek to kill me?"
Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
20 The crowd answered, "You have a demon. Who seeks to kill you?"
Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
21 Jesus answered them, "I did one work, and you are all amazed.
Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
22 Moses has given you circumcision (not that it is of Moses, but of the fathers), and on the Sabbath you circumcise a boy.
Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
23 If a boy receives circumcision on the Sabbath, that the Law of Moses may not be broken, are you angry with me, because I made a man completely healthy on the Sabbath?
Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
24 Do not judge according to appearance, but judge righteous judgment."
Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
25 Therefore some of them of Jerusalem said, "Is not this he whom they seek to kill?
Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
26 Look, he speaks openly, and they say nothing to him. Can it be that the rulers indeed know that this is the Christ?
Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
27 However we know where this man comes from, but when the Christ comes, no one will know where he comes from."
Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
28 Jesus therefore called out in the temple, teaching and saying, "You both know me, and know where I am from. I have not come of myself, but he who sent me is true, whom you do not know.
Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
29 I know him, because I am from him, and he sent me."
koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
30 They sought therefore to take him; but no one laid a hand on him, because his hour had not yet come.
Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
31 But many in the crowd believed in him. They said, "When the Christ comes, he won't do more signs than those which this man has done, will he?"
Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
32 The Pharisees heard the crowd murmuring these things concerning him, and the chief priests and the Pharisees sent officers to arrest him.
Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
33 Then Jesus said, "I will be with you a little while longer, then I go to him who sent me.
Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
34 You will seek me, but won't find; and where I am, you cannot come."
Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
35 The Jewish leaders therefore said among themselves, "Where will this man go that we won't find him? Will he go to the Diaspora among the Greeks, and teach the Greeks?
Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
36 What is this word that he said, 'You will seek me, but won't find; and where I am, you cannot come'?"
Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
37 Now on the last and greatest day of the feast, Jesus stood and said in a loud voice, "If anyone is thirsty, let him come to me and drink.
Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
38 He who believes in me, as the Scripture has said, from within him will flow rivers of living water."
Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
39 But he said this about the Spirit, which those believing in him were to receive. For the Spirit was not yet given, because Jesus was not yet glorified.
Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
40 Some of the crowd therefore, when they heard these words, said, "This is truly the Prophet."
Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
41 Others said, "This is the Christ." But some said, "What, does the Christ come out of Galilee?
Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
42 Hasn't the Scripture said that the Christ comes of the offspring of David, and from Bethlehem, the village where David was?"
Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
43 So there arose a division in the crowd because of him.
Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
44 Some of them would have arrested him, but no one laid hands on him.
Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
45 The officers therefore came to the chief priests and Pharisees, and they said to them, "Why did you not bring him?"
Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
46 The officers answered, "No man ever spoke like this man."
Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
47 The Pharisees therefore answered them, "You are not also led astray, are you?
Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
48 Have any of the rulers believed in him, or of the Pharisees?
“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
49 But this crowd that does not know the Law is accursed."
Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
50 Nicodemus (he who came to him before, being one of them) said to them,
Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
51 "Does our Law judge a man, unless it first hears from him personally and knows what he does?"
“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
52 They answered him, "Are you also from Galilee? Search, and see that no prophet comes from Galilee."
Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
53 Then everyone went to his own house,
Kenaka onse anachoka, napita kwawo.