< Hebrews 10 >
1 For the Law, having a shadow of the good to come, not the very image of the things, can never with the same sacrifices year by year, which they offer continually, make perfect those who draw near.
Malamulo ndi chithunzithunzi cha zinthu zabwino zimene zikubwera, osati madalitso enieniwo. Pa chifukwa chimenechi sizingatheke konse kuti nsembe zimodzimodzi, zoperekedwa kawirikawiri, kosalekeza ndi chaka ndi chaka, kuti nʼkusandutsa angwiro amene amabwera kudzapembedza.
2 Or else would not they have ceased to be offered, because the worshippers, having been once cleansed, would have had no more consciousness of sins?
Ngati zikanamatero iwowo akanasiya kupereka nsembezo. Pakuti opembedzawo akanamayeretsedwa kamodzi kokha, sibwenzi chikumbumtima chawo chikuwatsutsabe chifukwa cha machimo awo.
3 But in those sacrifices there is yearly reminder of sins.
Koma nsembezo zimawakumbutsa anthuwo machimo awo chaka ndi chaka.
4 For it is impossible that the blood of bulls and goats should take away sins.
Chifukwa nʼkosatheka kuti magazi angʼombe yayimuna ndi mbuzi yayimuna achotse machimo.
5 Therefore when he comes into the world, he says, "Sacrifice and offering you did not desire, but a body you prepared for me.
Nʼchifukwa chake Khristu atabwera pa dziko lapansi anati, “Simunafune nsembe kapena zopereka, koma thupi munandikonzera.
6 Whole burnt offerings and sin-offerings you took no pleasure in.
Simunakondwere nazo nsembe zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo.
7 Then I said, 'Look, I have come. It is written about me in the scroll of a book; to do your will, God.'"
Tsono, Ine ndinati, ‘Ndili pano Ine, Inu Mulungu, ndabwera kudzachita zimene mukufuna monga zinalembedwa mʼMalemba.’”
8 Previously saying, "Sacrifices and offerings and whole burnt offerings and sin-offerings you did not desire, nor took pleasure in" (which are offered according to the Law),
Poyamba Iye anati, “Nsembe kapena zopereka zopsereza ndi nsembe zopereka chifukwa cha tchimo, Inu simunazifune kapena kukondwera nazo.” Ngakhale kuti Malamulo ndiye amanena kuti ziperekedwe.
9 then he said, "Look, I have come to do your will." He takes away the first, that he may establish the second,
Pamenepo Iye anati, “Ndili pano Ine, ndabwera kudzachita zimene mukufuna.” Khristu anachotsa nsembe zoyamba zija kuti mʼmalo mwake ayikemo nsembe za mtundu wachiwiri.
10 by which will we have been sanctified through the offering of the body of Jesus Christ once for all.
Chifukwa chakuti Yesu Khristu anachita zimene Mulungu anafuna kuti achite, ndife oyeretsedwa ndi nsembe ya thupi lake, limene analipereka kamodzi kokha.
11 Every priest indeed stands day by day serving and often offering the same sacrifices, which can never take away sins,
Wansembe aliyense amayimirira tsiku ndi tsiku nʼkutumikira, ndipo amapereka nsembe imodzimodzi mobwerezabwereza, nsembe zimene sizingathe kuchotsa machimo.
12 but this one, when he had offered one sacrifice for sins forever, sat down on the right hand of God;
Koma pamene wansembe uyu anapereka kamodzi kokha nsembe imodzi yokha chifukwa cha machimo, Iye anakhala pansi ku dzanja lamanja la Mulungu.
13 from that time waiting until his enemies are made the footstool of his feet.
Kumeneko akudikira tsono kuti Mulungu asandutse adani ake kukhala chopondapo mapazi ake.
14 For by one offering he has perfected forever those who are being sanctified.
Chifukwa cha nsembe imodzi Iye anasandutsa angwiro kwamuyaya iwo amene akuwayeretsa.
15 The Holy Spirit also testifies to us, for after saying,
Mzimu Woyera nayenso akuchitira umboni za zimenezi kwa ife. Poyamba Iye anati,
16 "This is the covenant that I will make with them: 'After those days,' says the Lord, 'I will put my laws on their hearts, I will also write them on their minds.'"
“Ili ndi pangano limene ndidzachita nawo atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika malamulo anga mʼmitima mwawo, ndipo ndidzawalemba mʼmaganizo mwawo.”
17 "And I will remember their sins and their iniquities no more."
Ndipo akutinso: “Sindidzakumbukiranso konse machimo awo ndi zolakwa zawo.”
18 Now where forgiveness of these is, there is no more offering for sin.
Ndipo pamene machimo akhululukidwa, sipafunikanso nsembe yoperekedwa chifukwa cha machimowo.
19 Having therefore, brothers, boldness to enter into the holy place by the blood of Jesus,
Ndipo tsono abale, molimba mtima timalowa mʼMalo Opatulika kwambiri chifukwa cha magazi a Yesu.
20 by the way which he dedicated for us, a new and living way, through the curtain, that is to say, his flesh;
Iye anatitsekulira njira yatsopano ndi yamoyo kudutsa chinsalu chotchinga, chimene ndi thupi lake.
21 and having a great priest over the house of God,
Ndiponso tili ndi wansembe wamkulu woyangʼanira nyumba ya Mulungu.
22 let us draw near with a true heart in fullness of faith, having our hearts sprinkled from an evil conscience, and having our body washed with pure water,
Tsono tiyeni tiyandikire kwa Mulungu ndi mtima woona ndi wodzaza ndi chikhulupiriro. Popeza mitima yathu yayeretsedwa, ndi yopanda chikumbumtima chotitsutsa, ndiponso matupi athu asambitsidwa ndi madzi woyera.
23 let us hold fast the confession of our hope without wavering; for he who promised is faithful.
Tiyeni tigwiritsitse mosagwedezeka zimene timaziyembekezera ndi kuzivomereza, pakuti amene anatilonjezayo ndi wokhulupirika.
24 Let us consider how to motivate one another to love and good works,
Tiziganizira mmene tingalimbikitsirane wina ndi mnzake pokondana ndi kuchita ntchito zabwino.
25 not forsaking our own assembling together, as the custom of some is, but exhorting one another; and so much the more, as you see the Day approaching.
Tiyeni tisaleke kusonkhana kwathu pamodzi monga mmene ena amachitira, koma tizilimbikitsana makamaka poona kuti tsiku la Ambuye layandikira.
26 For if we sin willfully after we have received the knowledge of the truth, there remains no more a sacrifice for sins,
Ngati ife tipitirira kuchimwa mwadala pamene tikudziwa choona, palibenso nsembe ina imene ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.
27 but a certain fearful expectation of judgment, and a fierceness of fire which will devour the adversaries.
Koma kumangodikira kokha ndi mantha chiweruzo ndiponso moto woopsa umene udzawononga adani a Mulungu
28 Anyone who disregards the Law of Moses dies without compassion on the word of two or three witnesses.
Aliyense amene amakana malamulo a Mose amaphedwa popanda nʼchifundo chomwe, malingana pali mboni ziwiri kapena zitatu.
29 How much worse punishment, do you think, will he be judged worthy of, who has trodden under foot the Son of God, and has counted the blood of the covenant with which he was sanctified an unholy thing, and has insulted the Spirit of grace?
Koposa kotani nanga ululu wachilango chimene adzalandire munthu amene amapeputsa Mwana wa Mulungu, amene amayesa magazi a pangano, amene anamuyeretsa, kukhala chinthu chodetsedwa, ndi kunyoza Mzimu wachisomo?
30 For we know him who said, "Vengeance belongs to me; I will repay." Again, "The Lord will judge his people."
Pakuti timadziwa amene anati, “Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.” Iye anatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.”
31 It is a fearful thing to fall into the hands of the living God.
Nʼchinthu choopsa kugwa mʼmanja a Mulungu wamoyo.
32 But remember the former days, in which, after you were enlightened, you endured a great struggle with sufferings;
Kumbukirani masiku akale aja mutangowunikiridwa chatsopano, pa nthawi imeneyi munapirira zowawa zambiri.
33 partly, being exposed to insults and abuse in public, and sometimes you came to share with others who were treated in the same way.
Nthawi zina ankakunyozani pagulu ndi kukuzunzani. Nthawi zina munkamva zowawa pamodzi ndi amene ankasautsidwa chotere.
34 For you both had compassion on them that were in chains, and joyfully accepted the plundering of your possessions, since you knew that you yourselves had a better possession and an enduring one.
Munkawamvera chisoni amene anali mʼndende ndiponso munkalola mokondwera kuti akulandeni katundu wanu chifukwa munkadziwa kuti muli nacho chuma choposa ndi chosatha.
35 Therefore do not throw away your boldness, which has a great reward.
Tsono musataye kulimbika mtima kwanuko pakuti mudzalandira nako mphotho yayikulu.
36 For you need patient endurance so that, having done the will of God, you may receive the promise.
Nʼkofunika kuti mupirire kuti pamene muchita chifuniro cha Mulungu mudzalandire zimene Iye analonjeza.
37 "For in just a little while, he who is coming will come and will not delay.
Pakuti nʼkanthawi kochepa chabe, Iye amene akubwera adzabwera ndipo sadzachedwa ayi.
38 But the righteous will live by faith, and if he holds back, my soul has no pleasure in him."
Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro. Ndipo ngati iye abwerera mʼmbuyo chifukwa cha mantha, Ine sindidzakondwera naye.
39 But we are not of those who shrink back to destruction, but of those who have faith to the saving of the soul.
Koma ife sindife amodzi a iwo obwerera mʼmbuyo mwa mantha ndi owonongedwa, koma ndife amodzi a amene akukhulupirira ndi wopulumutsidwa.