< Matthew 10 >

1 And he called to himself his twelve disciples, and gave them authority over unclean spirits, to cast them out, and to heal every disease and every sickness.
Yesu anayitana ophunzira ake khumi ndi awiri ndipo anawapatsa ulamuliro otulutsa mizimu yoyipa ndi kuchiritsa nthenda iliyonse ndi zofowoka zilizonse.
2 Now the names of the twelve apostles are these. The first, Shimon, who is called Kipha; and Andreus his brother; and Yaquv the son of Zabedai, and Yukhanan his brother;
Mayina a atumwi khumi ndi awiriwo ndi awa: woyamba, Simoni (wotchedwa Petro) ndi mʼbale wake Andreya; Yakobo mwana wa Zebedayo ndi mʼbale wake Yohane,
3 Philipus and Bar-Tulmai; Tama and Mattai the tax collector; Yaquv the son of Khalphai, and Thadai;
Filipo ndi Bartumeyu, Tomasi ndi Mateyu wolandira msonkho, Yakobo mwana wa Alufeyo ndi Tadeyo;
4 Shimon the Zealot, and Yehudah Sekariuta, who also betrayed him.
Simoni Mzerote ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.
5 Yeshua sent these twelve out, and commanded them, saying, "Do not go among the non-Jews, and do not enter into any city of the Samaritans.
Yesu anatuma khumi ndi awiriwo ndi kuwalamula kuti, “Musapite kwa anthu a mitundu ina kapena kulowa mʼmudzi uliwonse wa Asamariya.
6 Rather, go to the lost sheep of the house of Israyel.
Koma pitani kwa nkhosa zotayika za banja la Israeli.
7 And as you go, proclaim, saying, 'The kingdom of heaven is near.'
Pamene mukupita, muzikalalikira uthenga uwu: ‘Ufumu wakumwamba wayandikira.’
8 Heal the sick, raise the dead, cleanse the lepers, cast out demons. Freely you received, freely give.
Chiritsani odwala, ukitsani akufa, chiritsani akhate, tulutsani ziwanda. Munalandira kwaulere, perekani kwaulere.
9 Do not take any gold, nor silver, nor copper in your money belts.
“Musatenge ndalama zagolide kapena zasiliva kapena zakopala mʼzikwama mwanu;
10 Take no bag for your journey, neither two tunics, nor shoes, nor staff: for the laborer is worthy of his food.
musatenge thumba la paulendo, kapena malaya awiri kapena nsapato kapena ndodo; pakuti wantchito ayenera kulandira chakudya chake.
11 And into whatever city or village you enter, find out who in it is worthy; and stay there until you go on.
Mukalowa mu mzinda ndi mʼmudzi uliwonse, funafunani munthu woyenera ndipo mukhale mʼnyumba mwake kufikira mutachoka.
12 And as you enter into the household, greet it.
Pamene mulowa mʼnyumba mupereke moni.
13 And if the household is worthy, let your peace come on it, but if it is not worthy, let your peace return to you.
Mtendere wanu ukhale pa a mʼnyumbayo ngati ndi oyenera. Koma ngati siwoyenera, mtendere wanu ubwerere kwa inu.
14 And whoever does not receive you, nor hear your words, as you leave that house or that city, shake off the dust from your feet.
Ngati wina aliyense sakakulandirani kapena sakamvera mawu anu, musase fumbi la kumapazi anu pamene mutuluka mʼnyumbayo kapena mu mzindawo.
15 Truly I tell you, it will be more tolerable for the land of Sedum and Amura in the day of judgment than for that city.
Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pa tsiku lachiweruziro, mlandu wa Sodomu ndi Gomora udzachepa kusiyana ndi wa mzindawo.
16 "Look, I send you out as sheep in the midst of wolves, so be cunning as snakes and innocent as doves.
“Taonani ndikukutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu. Chifukwa chake khalani ochenjera ngati njoka ndi woona mtima ngati nkhunda.
17 But beware of people: for they will deliver you up to councils, and in their synagogues they will scourge you.
Chenjerani ndi anthu pakuti adzakuperekani ku mabwalo amilandu nadzakukwapulani mʼmasunagoge mwawo.
18 Yes, and you will be brought before governors and kings for my sake, for a testimony to them and to the nations.
Chifukwa cha Ine, mudzaperekedwa kwa olamulira ndi kwa mafumu kuti mukhale mboni kwa iwo ndi kwa a mitundu ina.
19 But when they deliver you over, do not be anxious how or what you will say, for it will be given you in that hour what you will say.
Koma pamene akumangani, inu musadandaule kuti mukanena bwanji kapena mukanena chiyani. Mudzapatsidwa pa nthawi imeneyo zoti munene,
20 For it is not you who speak, but the Rukha of your Father who speaks in you.
pakuti sindinu mudzanena, koma Mzimu Woyera wa Atate anu, adzayankhula mwa inu.
21 "And brother will deliver up brother to death, and the father his child. Children will rise up against parents, and cause them to be put to death.
“Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe ndi abambo mwana wawo: ndipo ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe.
22 And you will be hated by everyone because of my name, but the one who perseveres to the end will be saved.
Anthu onse adzada inu chifukwa cha Ine, koma iye amene apirira mpaka kumapeto, adzapulumuka.
23 But when they persecute you in one city, flee to the other. And if they persecute you in the other, flee to the next. For truly I tell you, you will not have gone through the cities of Israyel before the Son of Man comes.
Pamene akuzunzani pamalo ena thawirani kwina. Pakuti ndikuwuzani zoonadi kuti simudzamaliza mizinda yonse ya Israeli Mwana wa Munthu asanabwere.
24 "A disciple is not above the teacher, nor a servant above his lord.
“Wophunzira saposa mphunzitsi wake ndipo wantchito saposa bwana wake.
25 It is enough for the disciple that he be like his teacher, and the servant like his lord. If they have called the master of the house Baelzebub, how much more those of his household.
Nʼkoyenera kuti wophunzira akhale ngati mphunzitsi wake, ndi wantchito akhale ngati bwana wake. Ngati mwini banja atchedwa Belezebabu, koposa kotani a mʼnyumba mwake!
26 Therefore do not be afraid of them, for there is nothing covered that will not be revealed; and hidden that will not be known.
“Chifukwa chake musaope iwo. Pakuti palibe chinthu chobisika chimene sichidzavundukulidwa, ndi chobisika chimene sichidzadziwika.
27 What I tell you in the darkness, speak in the light; and what you hear whispered in the ear, proclaim on the housetops.
Chimene ndikuwuzani Ine mu mdima, muchiyankhule poyera; chimene akunongʼonezani mʼkhutu, muchilalikire muli pa denga.
28 And do not be afraid of those who kill the body, but are not able to kill the soul. Rather, fear him who is able to destroy both soul and body in Gihana. (Geenna g1067)
Musamaope amene amapha thupi koma sangathe kuchotsa moyo. Koma muziopa Iye amene akhoza kupha mzimu ndi kuwononga thupi mu gehena. (Geenna g1067)
29 "Are not two sparrows sold for an asarah coin? Not one of them falls on the ground apart from your Father's will,
Kodi suja amagulitsa mbalame ziwiri ndi ndalama imodzi? Koma palibe imodzi ya izo imene idzagwa pansi wopanda chifuniro cha Atate anu.
30 but the very hairs of your head are all numbered.
Ndipo ngakhale tsitsi la mʼmutu mwanu linawerengedwa kale.
31 Therefore do not be afraid. You are of more value than many sparrows.
Potero musaope; inu ndinu a mtengo woposa mbalame zambiri.
32 Everyone therefore who confesses me before people, him I will also confess before my Father who is in heaven.
“Aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzavomereza pamaso pa Atate anga akumwamba.
33 But whoever denies me before people, him I will also deny before my Father who is in heaven.
Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzamukana pamaso pa Atate anga akumwamba.
34 "Do not think that I came to send peace on the earth. I did not come to send peace, but a sword.
“Musaganize kuti Ine ndabweretsa mtendere pa dziko lapansi. Sindinabwere kudzapereka mtendere koma lupanga.
35 For I came to set a man at odds against his father, and a daughter against her mother, and a daughter-in-law against her mother-in-law.
Pakuti Ine ndabwera kudzalekanitsa “‘Munthu ndi abambo ake, mwana wamkazi ndi amayi ake, mtengwa kulekanitsidwa ndi apongozi ake,
36 And a person's foes will be those of his own household.
adani a munthu adzakhala a mʼbanja mwake momwe.’
37 Whoever loves father or mother more than me is not worthy of me; and whoever loves son or daughter more than me is not worthy of me.
“Aliyense amene akonda abambo kapena amayi ake koposa Ine sayenera kukhala wanga; aliyense amene akonda mwana wake wamwamuna kapena wamkazi koposa Ine sayenera kukhala wanga.
38 And whoever does not take his cross and follow after me, is not worthy of me.
Aliyense amene satenga mtanda wake ndi kunditsata Ine sayenera kukhala wanga.
39 Whoever seeks his life will lose it; and whoever loses his life for my sake will find it.
Aliyense amene asunga moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo chifukwa cha Ine adzawupeza.
40 Whoever receives you receives me, and whoever receives me receives him who sent me.
“Iye amene alandira inu alandira Ine, ndipo amene alandira Ine alandiranso amene anandituma Ine.
41 The one who receives a prophet because he is a prophet will receive a prophet's reward, and the one who receives a righteous person because he is a righteous person will receive a righteous person's reward.
Aliyense amene alandira mneneri chifukwa chakuti ndi mneneri alandira mphotho ya mneneri, ndipo aliyense amene alandira munthu wolungama chifukwa chakuti ndi munthu wolungama, adzalandira mphotho ya wolungama.
42 And whoever gives one of these little ones just a cup of cold water to drink because he is a disciple, truly I tell you he will in no way lose his reward."
Ngati aliyense apereka madzi ozizira a mʼchikho kwa mmodzi wa angʼonoangʼono awa chifukwa cha kuti ndi ophunzira anga, ndikuwuzani zoona, ndithudi sadzataya mphotho yake.”

< Matthew 10 >