< Hebrews 11 >

1 Now faith is being confident of what we hope for, convinced about things we do not see.
Tsopano chikhulupiriro ndi kusakayika konse pa zinthu zimene tikuziyembekeza, ndi kutsimikiza kuti zinthu zimene sitiziona zilipo ndithu.
2 For by this, the people of old were attested.
Ndi chikhulupiriro chimenechi makolo athu akale anayamikidwa.
3 By faith, we understand that the ages were prepared by the word of God, so that what is seen has not been made out of things which are visible. (aiōn g165)
Ndi chikhulupiriro timazindikira kuti dziko lapansi ndi la mmwamba zinapangidwa ndi Mawu a Mulungu, ndikuti zinthu zoonekazi zinachokera ku zinthu zosaoneka. (aiōn g165)
4 By faith, Habeil offered to God a better sacrifice than Qayen, through which he was attested as righteous, God testifying with respect to his gifts; and though he died he still speaks through it.
Ndi chikhulupiriro Abele anapereka kwa Mulungu nsembe yoposa imene Kaini anapereka. Ndi chikhulupiriro anatchedwa munthu wolungama Mulungu atayamikira zopereka zake. Ngakhale iye anafa, akuyankhulabe chifukwa cha chikhulupiriro chakecho.
5 By faith, Khenuk was taken away, so that he would not see death, "and he was not found, because God took him away." For before he was taken he was attested as having pleased God.
Ndi chikhulupiriro Enoki anatengedwa wamoyo, motero iye sanalawe imfa; sanapezeke chifukwa Mulungu anamutenga. Pakuti asanatengedwe anayamikiridwa kuti ankakondweretsa Mulungu.
6 Now without faith it is impossible to be well pleasing to him, for he who comes to God must believe that he exists, and that he is a rewarder of those who seek him.
Ndipo popanda chikhulupiriro nʼkosatheka kukondweretsa Mulungu, chifukwa aliyense amene amabwera kwa Iye ayenera kukhulupirira kuti Mulungu alipodi ndi kuti Iye amapereka mphotho kwa amene akumufunitsitsa.
7 By faith, Nukh, being warned about things not yet seen, in reverence prepared a box-shaped ship for the salvation of his household, through which he condemned the world, and became heir of the righteousness which is according to faith.
Ndi chikhulupiriro, Nowa atachenjezedwa za zinthu zimene zinali zisanaoneke, anachita mantha napanga chombo kuti apulumutsire banja lake. Ndi chikhulupiriro chake anatsutsa dziko lapansi ndipo analandira chilungamo chimene chimabwera ndi chikhulupiriro.
8 By faith, Avraham, when he was called, obeyed to go out to a place which he was to receive for an inheritance. He went out, not knowing where he was going.
Ndi chikhulupiriro Abrahamu atayitanidwa kuti apite ku dziko limene anamulonjeza kuti lidzakhala lake, anamvera ndi kupita, ngakhale sanadziwe kumene ankapita.
9 By faith, he sojourned in a land of promise, as a foreigner, living in tents with Iskhaq and Yaquv, the heirs with him of the same promise.
Ndi chikhulupiriro chomwecho anakhala ngati mlendo mʼdziko lija limene Mulungu anamulonjeza. Anakhala mʼmatenti monganso anachitira Isake ndi Yakobo, amene nawonso analonjezedwanso.
10 For he looked for the city which has foundations, whose architect and builder is God.
Pakuti amadikira mudzi wokhala ndi maziko, umene mmisiri ndi womanga wake ndi Mulungu.
11 By faith, even barren Sarah herself received power to conceive when she was past age, and gave birth, since she considered him faithful who had promised.
Ndi chikhulupiriro Sara analandira mphamvu zokhala ndi pakati ngakhale kuti zaka zake zobala mwana zinali zitapita kale, popeza anamutenga amene analonjeza kukhala wokhulupirika.
12 Therefore as many as the stars of the sky in multitude, and as innumerable as the sand which is by the sea shore, were fathered by one man, and him as good as dead.
Nʼchifukwa chake mwa munthu mmodzi, amene anali ngati wakufa, munatuluka mibado yochuluka ngati nyenyezi ndi yosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
13 These all died in faith, not having received the promises, but having seen them and embraced them from afar, and having acknowledged that they were foreigners and temporary residents on the earth.
Onsewa anakhalabe mwachikhulupiriro mpaka anafa. Iwo sanalandire zimene Mulungu anawalonjeza; iwo anangozionera chapatali ndi kuzilandira. Ndipo iwo anavomereza kuti analidi alendo ndi osakhazikika pa dziko lapansi.
14 For those who say such things make it clear that they are seeking a country of their own.
Anthu amene amanena zinthu zotere amaonekeratu kuti akufuna dziko lawo lenileni.
15 If indeed they had been thinking of that country from which they went out, they would have had enough time to return.
Akanakhala kuti akuganizira za dziko limene analisiya akanapeza mpata obwerera kwawo.
16 Instead, they were longing for a better country, that is, a heavenly one. Therefore God is not ashamed of them, to be called their God, for he has prepared a city for them.
Mʼmalo mwake, iwo amafunitsitsa dziko labwino, ndilo lakumwamba. Nʼchifukwa chake Mulungu sachita manyazi kutchedwa Mulungu wawo, pakuti Iye anawalonjeza mudzi.
17 By faith, Avraham, being tested, offered up Iskhaq; and he who had gladly received the promises was offering up his one and only son;
Ndi chikhulupiriro Abrahamu, Mulungu atamuyesa, anapereka Isake ngati nsembe. Ngakhale anali munthu woti Mulungu anamulonjeza, anakhala wokonzeka kupereka nsembe mwana wake mmodzi yekhayo.
18 even he to whom it was said, "In Iskhaq will your descendants be called;"
Za mwana ameneyu Mulungu anamuwuza iye kuti, “Zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.”
19 concluding that God is able to raise up even from the dead. Figuratively speaking, he also did receive him back from the dead.
Abrahamu amazindikira kuti Mulungu angathe kuukitsa akufa, ndipo tingathe kunena mofanizira kuti iye analandiranso Isake ngati wouka kwa akufa.
20 By faith, Iskhaq blessed Yaquv and Isuw, even concerning things to come.
Ndi chikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau pa zatsogolo lawo.
21 By faith, Yaquv, when he was dying, blessed each of the sons of Yauseph, and bowed over the top of his staff.
Ndi chikhulupiriro, pamene Yakobo ankamwalira anadalitsa ana awiri a Yosefe, ndipo anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
22 By faith, Yauseph, when his end was near, made mention of the departure of the people of Israyel; and gave instructions concerning his bones.
Ndi chikhulupiriro Yosefe ali pafupi kumwalira anayankhula za kutuluka kwa Aisraeli mu Igupto ndipo anawawuza zoti adzachite ndi mafupa ake.
23 By faith, Mushe, when he was born, was hidden for three months by his parents, because they saw that he was a beautiful child, and they were not afraid of the king's commandment.
Ndi chikhulupiriro Mose atabadwa makolo ake anamubisa miyezi itatu, chifukwa iwo anaona kuti mwanayo anali wokongola ndipo sanaope konse lamulo la mfumu.
24 By faith, Mushe, when he had grown up, refused to be called the son of Pharaoh's daughter,
Ndi chikhulupiriro Mose atakula, anakana kutchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao.
25 choosing rather to share ill treatment with God's people, than to enjoy the pleasures of sin for a time;
Iye anasankha kuzunzika nawo limodzi anthu a Mulungu kuposa kusangalala ndi zokondweretsa za uchimo kwa nthawi yochepa.
26 considering the abuse suffered for the Meshikha greater riches than the treasures of Egypt; for he looked to the reward.
Anaona kuti kuzunzika chifukwa cha Khristu kunali kwa mtengowapatali kuposa chuma cha ku Igupto, chifukwa amaona mphotho ya mʼtsogolo.
27 By faith, he left Egypt, not fearing the wrath of the king; for he endured, as seeing him who is invisible.
Ndi chikhulupiriro anachoka ku Igupto wosaopa ukali wa mfumu. Iye anapirira chifukwa anamuona Mulungu amene ndi wosaonekayo.
28 By faith, he kept the Passover, and the sprinkling of the blood, that the destroyer of the firstborn should not touch them.
Ndi chikhulupiriro anachita Paska ndi kuwaza magazi, kuti mngelo wowononga ana oyamba kubadwa asaphe ana oyamba kubadwa a Aisraeli.
29 By faith, they passed through the Red Sea as on dry land. When the Egyptians tried to do so, they were swallowed up.
Ndi chikhulupiriro Aisraeli anawoloka Nyanja Yofiira ngati pa mtunda powuma, koma Aigupto atayesa kutero anamizidwa.
30 By faith, the walls of Irikhu fell down, after they had been encircled for seven days.
Ndi chikhulupiriro mpanda wa Yeriko unagwa, Aisraeli atawuzungulira kasanu ndi kawiri.
31 By faith, Rakhav the prostitute did not perish with those who were disobedient, having received the spies in peace.
Ndi chikhulupiriro Rahabe, mkazi wadama sanaphedwe pamodzi ndi osamvera aja chifukwa analandira bwino ozonda aja ku nyumba kwake.
32 What more shall I say? For the time would fail me if I told of Gedeun, Baraq, Shemshun, Naphtakh, Dawid, Shemuyel, and the prophets;
Kodi ndinenenso chiyani? Nthawi yandichepera yoti ndinene za Gideoni, Baraki, Samsoni, Yefita, Davide, Samueli ndi aneneri,
33 who, through faith subdued kingdoms, worked out righteousness, obtained promises, stopped the mouths of lions,
amene ndi chikhulupiriro anagonjetsa mafumu, anakhazikitsa chilungamo ndi kulandira zimene zinalonjezedwa. Anatseka pakamwa pa mikango,
34 quenched the power of fire, escaped the edge of the sword, from weakness were made strong, grew mighty in war, and caused foreign armies to flee.
anazimitsa moto waukali, ndipo anapulumuka osaphedwa ndi lupanga. Anali ofowoka koma analandira mphamvu; anasanduka amphamvu pa nkhondo, nathamangitsa magulu a ankhondo a adani awo.
35 Women received their dead by resurrection. And others were tortured, not accepting the payment for release, that they might obtain a better resurrection.
Amayi ena analandira anthu awo amene anafa, ataukitsidwanso. Enanso anazunzidwa ndipo anakana kumasulidwa, kuti adzaukenso ndi moyo wabwino.
36 Others were tried by mocking and scourging, yes, moreover by bonds and imprisonment.
Ena anawaseka ndi kuwakwapula, pamenenso ena anamangidwa ndi kupita ku ndende.
37 They were stoned, they were sawed apart, they were put to the test, they were killed with the sword. They went around in sheepskins and in goatskins, being destitute, afflicted, mistreated
Anagendedwa miyala; anachekedwa pakati; ena anaphedwa ndi lupanga. Iwo anayendayenda atavala zikopa zankhosa ndi zikopa zambuzi, umphawi okhaokha, ozunzidwa ndi kuvutitsidwa.
38 (of whom the world was not worthy), wandering in deserts, mountains, caves, and the holes of the earth.
Dziko lapansi silinawayenere. Anayendayenda mʼzipululu ndi mapiri, ndiponso mʼmapanga ndi mʼmaenje.
39 These all, having had testimony given to them through their faith, did not receive the promise,
Onsewa anayamikidwa chifukwa cha chikhulupiriro chawo, komabe palibe wa iwo amene analandira zimene analonjezedwa.
40 God having provided some better thing concerning us, so that apart from us they should not be made perfect.
Mulungu anatikonzera ife kanthu koposa, kuti iwo asayesedwe angwiro popanda ife.

< Hebrews 11 >