< Acts 2 >

1 Now when the day of Pentecost had come, they were all together in one place.
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 Suddenly there came from the sky a sound like the rushing of a mighty wind, and it filled all the house where they were sitting.
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 Tongues like fire appeared and were distributed to them, and one sat on each of them.
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 They were all filled with the Rukha d'Qudsha, and began to speak in other languages, as the Rukha enabled them to speak out.
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 Now there were dwelling in Urishlim Jews, devout people from every nation under the sky.
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 When this sound was heard, the crowd came together, and were bewildered, because everyone heard them speaking in his own language.
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 They were all amazed and marveled, saying, "Look, are not all these who speak Galilaye?
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 How do we hear, everyone in our own native language?
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 Parthians, Medes, Elamites, and people from Mesopotamia, Yehuda, Cappadocia, Pontus, Asia,
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 Phrygia, Pamphylia, Egypt, the parts of Libya around Qurini, visitors from Rome, both Jews and proselytes,
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 Cretans and Arabians: we hear them speaking in our tongues the mighty works of God."
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 They were all amazed, and were perplexed, saying one to another, "What does this mean?"
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 Others, mocking, said, "They are filled with new wine."
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 But Kipha, standing up with the eleven, lifted up his voice, and spoke out to them, "You men of Yehuda, and all you who live in Urishlim, let this be known to you, and listen to my words.
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 For these are not drunk, as you suppose, seeing it is only nine in the morning.
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 But this is what has been spoken through the prophet Joel:
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 'And it will be in the last days, says God, that I will pour out my Rukha on all flesh; and your sons and your daughters will prophesy, and your young men will see visions, and your old men will dream dreams.
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 And even on my servants, both men and women, I will pour out my Rukha in those days, and they will prophesy.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 And I will show wonders in the sky above, and signs on the earth beneath; blood, and fire, and billows of smoke.
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 The sun will be turned into darkness, and the moon into blood, before the great and glorious day of the Lord comes.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 And it will be that whoever will call on the name of the Lord will be saved.'
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 "Men of Israyel, hear these words. Yeshua the Natsraya, a man approved by God to you by mighty works and wonders and signs which God did by him in the midst of you, even as you yourselves know,
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 him, being delivered up by the determined counsel and foreknowledge of God, by the hand of lawless men, crucified and killed;
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 whom God raised up, having freed him from the pains of death, because it was not possible that he should be held by it.
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 For Dawid says concerning him, 'I saw the Lord always before me, for he is at my right hand, that I should not be shaken.
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 Therefore my heart was glad, and my tongue rejoiced, and moreover my flesh also will dwell in hope;
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 because you will not leave my soul in Sheyul, neither will you allow your Holy One to see decay. (Hadēs g86)
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
28 You made known to me the paths of life. You will make me full of joy in your presence.'
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 "Brothers, I may tell you freely of the patriarch Dawid, that he both died and was buried, and his tomb is with us to this day.
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 Therefore, being a prophet, and knowing that God had sworn with an oath to him that one of his descendants would sit on his throne,
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 he foreseeing this spoke about the resurrection of the Meshikha, that neither was he left in Sheyul, nor did his flesh see decay. (Hadēs g86)
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
32 This Yeshua God raised up, to which we all are witnesses.
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 Being therefore exalted by the right hand of God, and having received from the Father the promise of the Rukha d'Qudsha, he has poured out this, which you see and hear.
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 For Dawid did not ascend into the heavens, but he says himself, 'The Lord said to my Lord, "Sit by my right hand,
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 until I make your enemies a footstool for your feet."'
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 "Let all the house of Israyel therefore know certainly that God has made him both Lord and Meshikha, this Yeshua whom you crucified."
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 Now when they heard this, they were acutely distressed, and said to Kipha and the rest of the apostles, "Brothers, what shall we do?"
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 Kipha said to them, "Repent, and be baptized, every one of you, in the name of Yeshua Meshikha for the forgiveness of your sins, and you will receive the gift of the Rukha d'Qudsha.
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 For to you is the promise, and to your children, and to all who are far off, even as many as the Lord our God will call to himself."
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 With many other words he testified, and exhorted them, saying, "Save yourselves from this crooked generation."
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 Then those who received his word were baptized. There were added that day about three thousand souls.
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 They continued steadfastly in the apostles' teaching and fellowship, in the breaking of bread, and prayer.
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 Fear came on every soul, and many wonders and signs were done through the apostles.
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 All who believed were together, and had all things in common.
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 They sold their possessions and goods, and distributed them to all, according as anyone had need.
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 Day by day, continuing steadfastly with one accord in the temple, and breaking bread at home, they took their food with gladness and singleness of heart,
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 praising God, and having favor with all the people. The Lord added to their number day by day those who were being saved.
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.

< Acts 2 >