< Zechariah 7 >

1 And it comes to pass, in the fourth year of Darius the king, a word of YHWH has been to Zechariah, in the fourth of the ninth month, in Chisleu.
Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
2 And Beth-El sends Sherezer and Regem-Melech, and its men, to appease the face of YHWH,
Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
3 speaking to the priests who [are] at the house of YHWH of Hosts, and to the prophets, saying, “Do I weep in the fifth month—being separated—as I have done these so many years?”
pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
4 And there is a word of YHWH of Hosts to me, saying,
Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
5 “Speak to all the people of the land, and to the priests, saying,
“Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
6 When you fasted with mourning in the fifth and in the seventh [months]—even these seventy years—did you keep the fast [to] Me? And when you eat, and when you drink, is it not you who are eating, and you who are drinking?
Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
7 Are [these] not the words that YHWH proclaimed by the hand of the former prophets, in Jerusalem’s being inhabited, and [in] safety, and its cities around it, and the south and the plain—abiding?”
Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
8 And there is a word of YHWH to Zechariah, saying,
Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
9 “Thus spoke YHWH of Hosts, saying, Judge [with] true judgment, And do kindness and mercy with one another.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
10 And do not oppress widow, and fatherless, Sojourner, and poor, And you do not devise the calamity of one another in your heart.
Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
11 And they refuse to attend, And they give a stubborn shoulder, And their ears are made heavy against hearing.
“Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
12 And their heart they have made adamant, Against hearing the Law, and the words, That YHWH of Hosts sent by His Spirit, By the hand of the former prophets, And there is great wrath from YHWH of Hosts.
Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
13 And it comes to pass, as He called, And they have not listened, So they call, and I do not listen,” said YHWH of Hosts.
“‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
14 “And I toss them on all the nations, That they have not known, The land has been desolate behind them, Of any passing by and turning back, And they set a desirable land for a desolation!”
‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”

< Zechariah 7 >