< Psalms 9 >
1 TO THE OVERSEER. [SET] ON “DEATH OF THE SON.” A PSALM OF DAVID. I confess, O YHWH, with all my heart, I recount all Your wonders,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 I rejoice and exult in You, I praise Your Name, O Most High.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 In my enemies turning backward, They stumble and perish from Your face.
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 For You have done my judgment and my right. You have sat on a throne, Judging [with] righteousness.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 You have rebuked nations, You have destroyed the wicked, You have blotted out their name for all time and forever.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 The enemy—[your] destructions have been completed forever, As for cities you have plucked up, Their memorial has perished with them.
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 And YHWH abides for all time, He is preparing His throne for judgment.
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 And He judges the world in righteousness, He judges the peoples in uprightness.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 And YHWH is a tower for the bruised, A tower for times of adversity.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 They trust in You who know Your Name, For You have not forsaken those seeking You, O YHWH.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Sing praise to YHWH, inhabiting Zion, Declare His acts among the peoples,
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 For He who is seeking for blood Has remembered them, He has not forgotten the cry of the afflicted.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Favor me, O YHWH, See my affliction by those hating me, You who lift me up from the gates of death,
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 So that I recount all Your praise, In the gates of the daughter of Zion. I rejoice on Your salvation.
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Nations have sunk in a pit they made, Their foot has been captured in a net that they hid.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 YHWH has been known, He has done judgment; By a work of his hands The wicked has been snared. (Meditation, Selah)
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 The wicked turn back to Sheol, All nations forgetting God. (Sheol )
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol )
18 For the needy is not forgotten forever, [Nor] the hope of the humble lost for all time.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Rise, O YHWH, do not let man be strong, Let nations be judged before Your face.
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Appoint them to fear, O YHWH, Let nations know they [are] men! (Selah)
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)