< Psalms 78 >

1 AN INSTRUCTION OF ASAPH. Give ear, O my people, to my law, Incline your ear to sayings of my mouth.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 I open my mouth with an allegory, I bring forth hidden things of old,
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 That we have heard and know, And our fathers have recounted to us.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 We do not hide from their sons, Recounting praises of YHWH to a later generation, And His strength, and His wonders that He has done.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 And He raises up a testimony in Jacob, And has placed a law in Israel, That He commanded our fathers, To make them known to their sons.
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 So that a later generation knows, Sons who are born, rise and recount to their sons,
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 And place their confidence in God, And do not forget the doings of God, But keep His commands.
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 And they are not like their fathers, A generation apostatizing and being rebellious, A generation—it has not prepared its heart, Nor [is] its spirit steadfast with God.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Sons of Ephraim—armed bearers of bow, Have turned in a day of conflict.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 They have not kept the covenant of God, And they have refused to walk in His law,
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 And they forget His doings, And His wonders that He showed them.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 He has done wonders before their fathers, In the land of Egypt—the field of Zoan.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 He cleft a sea, and causes them to pass over, Indeed, He causes waters to stand as a heap.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 And leads them with a cloud by day, And with a light of fire all the night.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 He cleaves rocks in a wilderness, And gives drink—as the great deep.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 And brings out streams from a rock, And causes waters to come down as rivers.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 And they still add to sin against Him, To provoke the Most High in the dry place.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 And they try God in their heart, To ask food for their lust.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 And they speak against God—they said: “Is God able to array a table in a wilderness?”
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Behold, He has struck a rock, And waters flow, indeed, streams overflow. “Also, [is] He able to give bread? Does He prepare flesh for His people?”
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Therefore YHWH has heard, And He shows Himself angry, And fire has been kindled against Jacob, And anger has also gone up against Israel,
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 For they have not believed in God, Nor have they trusted in His salvation.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 And He commands clouds from above, Indeed, He has opened doors of the heavens.
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 And He rains manna on them to eat, Indeed, He has given grain of the heavens to them.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Each has eaten food of the mighty, He sent provision to them to satiety.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 He causes an east wind to journey in the heavens, And leads a south wind by His strength,
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 And He rains on them flesh as dust, And as sand of the seas—winged bird,
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 And causes [it] to fall in the midst of His camp, Around His dwelling places.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 And they eat, and are greatly satisfied, And He brings their desire to them.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 They have not been estranged from their desire, Their food [is] yet in their mouth,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 And the anger of God has gone up against them, And He slays among their fat ones, And He caused youths of Israel to bend.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 With all this they have sinned again, And have not believed in His wonders.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 And He consumes their days in vanity, And their years in trouble.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 If He slew them, then they sought Him, And turned back, and earnestly sought God,
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 And they remember that God [is] their rock, And God Most High their redeemer.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 And they deceive Him with their mouth, And lie to Him with their tongue,
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 And their heart has not been right with Him, And they have not been steadfast in His covenant.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 And He, the Merciful One, pardons iniquity, and does not destroy, And has often turned back His anger, And does not awaken all His fury.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 And He remembers that they [are] flesh, A wind going on—and it does not return.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 How often do they provoke Him in the wilderness, Grieve Him in the desolate place?
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Indeed, they turn back, and try God, And have limited the Holy One of Israel.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 They have not remembered His hand The day He ransomed them from the adversary.
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 When He set His signs in Egypt, And His wonders in the field of Zoan,
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 And He turns their streams to blood, And they do not drink their floods.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 He sends among them the beetle, and it consumes them, And the frog, and it destroys them,
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 And gives their increase to the caterpillar, And their labor to the locust.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 He destroys their vine with hail, And their sycamores with frost,
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 And delivers their beasts up to the hail, And their livestock to the burning flames.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 He sends on them the fury of His anger, Wrath, and indignation, and distress—A discharge of evil messengers.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 He ponders a path for His anger, He did not keep back their soul from death, Indeed, He delivered up their life to the pestilence.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 And He strikes every firstborn in Egypt, The first-fruit of the strong in tents of Ham.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 And causes His people to journey as a flock, And guides them as a drove in a wilderness,
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 And He leads them confidently, And they have not been afraid, And the sea has covered their enemies.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 And He brings them to the border of His sanctuary, This mountain His right hand had acquired,
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 And casts out nations from before them, And causes them to fall in the line of inheritance, And causes the tribes of Israel to dwell in their tents,
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 And they tempt and provoke God Most High, And have not kept His testimonies.
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 And they turn back, And deal treacherously like their fathers, They have been turned like a deceitful bow,
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 And make Him angry with their high places, And make Him zealous with their carved images,
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 God has heard, and shows Himself angry. And kicks exceedingly against Israel.
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 And He leaves the Dwelling Place of Shiloh, The tent He had placed among men,
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 And He gives His strength to captivity, And His beauty into the hand of an adversary,
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 And delivers His people up to the sword, And showed Himself angry with His inheritance.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Fire has consumed His young men, And His virgins have not been praised.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 His priests have fallen by the sword, And their widows do not weep.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 And the Lord wakes as a sleeper, As a mighty one crying aloud from wine.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 And He strikes His adversaries backward, He has put a continuous reproach on them,
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 And He kicks against the tent of Joseph, And has not fixed on the tribe of Ephraim.
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 And He chooses the tribe of Judah, With Mount Zion that He loved,
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 And builds His sanctuary as a high place, Like the earth, He founded it for all time.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 And He fixes on His servant David, And takes him from the folds of a flock,
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 He has brought him in from behind suckling ones, To rule over Jacob His people, And over Israel His inheritance.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 And he rules them according to the integrity of his heart, And leads them by the skillfulness of his hands!
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< Psalms 78 >