< Psalms 72 >

1 BY SOLOMON. O God, give Your judgments to the king, And Your righteousness to the king’s Son.
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 He judges Your people with righteousness, And Your poor with judgment.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 The mountains bear peace to the people, And the heights by righteousness.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 He judges the poor of the people, Gives deliverance to the sons of the needy, And bruises the oppressor.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 They fear You with the sun, and before the moon, Generation—generations.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 He comes down as rain on mown grass, As showers—sprinkling the earth.
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 The righteous flourish in His days, And abundance of peace until the moon is not.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 And He rules from sea to sea, And from the river to the ends of the earth.
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 Desert-dwellers bow before Him, And His enemies lick the dust.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 Kings of Tarshish and of the islands send back a present. Kings of Sheba and Seba bring a reward near.
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 And all kings bow themselves to Him, All nations serve Him,
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 For He delivers the needy who cries, And the poor when he has no helper,
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 He has pity on the poor and needy, And He saves the souls of the needy,
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 He redeems their soul from fraud and from violence, And their blood is precious in His eyes.
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 And He lives, and the gold of Sheba [is] given to Him, And prayer is continually made for Him, All day He is continually blessed.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 There is a handful of grain in the earth, On the top of mountains, Its fruit shakes like Lebanon, And they flourish out of the city as the herb of the earth.
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 His Name is for all time, Before the sun is His Name continued, And they bless themselves in Him, All nations pronounce Him blessed.
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Blessed is YHWH God, God of Israel, He alone is doing wonders,
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 And blessed [is] the Name of His glory for all time, And the whole earth is filled [with] His glory. Amen and amen!
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 The prayers of David son of Jesse have been ended.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

< Psalms 72 >