< Psalms 70 >

1 TO THE OVERSEER. BY DAVID. “TO CAUSE TO REMEMBER.” O God, [hurry] to deliver me, O YHWH, hurry to help me.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2 Let them be ashamed and confounded Who are seeking my soul, Let them be turned backward and blush Who are desiring my evil.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
3 Let them turn back because of their shame, Who are saying, “Aha, aha.”
Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4 Let all those seeking You rejoice and be glad in You, And let those loving Your salvation Continually say, “God is magnified.”
Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5 And I [am] poor and needy, O God, hurry to me, You [are] my help and my deliverer, O YHWH, do not linger!
Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.

< Psalms 70 >