< Psalms 50 >

1 A PSALM OF ASAPH. The God of gods—YHWH—has spoken, And He calls to the earth From the rising of the sun to its going in.
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 From Zion, the perfection of beauty, God shone.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Our God comes, and is not silent, Fire devours before Him, And around Him it has been very tempestuous.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 He calls to the heavens from above, And to the earth, to judge His people.
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Gather My saints to Me, Making covenant with Me over a sacrifice.
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 And the heavens declare His righteousness, For God Himself is judging. (Selah)
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Hear, O My people, and I speak, O Israel, and I testify against you, God—I [am] your God.
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 I do not reprove you for your sacrifices, Indeed, your burnt-offerings [Are] continually before Me.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 I do not take a bullock from your house, [Or] male goats from your folds.
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 For every beast of the forest [is] Mine, The livestock on the hills of oxen.
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 I have known every bird of the mountains, And the wild beast of the field [is] with Me.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 If I am hungry I do not tell [it] to you, For the world and its fullness [is] Mine.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Do I eat the flesh of bulls, And drink the blood of male goats?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 Sacrifice to God confession, And complete your vows to the Most High.
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 And call Me in a day of adversity, I deliver you, and you honor Me.
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 And to the wicked God has said: What to you—to recount My statutes? That you lift up My covenant on your mouth?
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Indeed, you have hated instruction, And cast My words behind you.
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 If you have seen a thief, Then you are pleased with him, And your portion [is] with adulterers.
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 You have sent forth your mouth with evil, And your tongue joins deceit together,
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 You sit, you speak against your brother, You give slander against a son of your mother.
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 These you did, and I kept silent, You have thought that I am like you, I reprove you, and set in array before your eyes.
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Now understand this, You who are forgetting God, Lest I tear, and there is no deliverer.
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 He who is sacrificing praise honors Me, As for him who makes a way, I cause him to look on the salvation of God!
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”

< Psalms 50 >