< Psalms 48 >
1 A SONG. A PSALM OF THE SONS OF KORAH. Great [is] YHWH, and greatly praised, In the city of our God—His holy hill.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Beautiful [for] elevation, A joy of all the land, [is] Mount Zion, The sides of the north, the city of [the] great King.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 God is known for a tower in her high places.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 For behold, the kings met, they passed by together,
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 They have seen—so they have marveled, They have been troubled, they were hurried away.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 Trembling has seized them there, Pain, as of a travailing woman.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 By an east wind You shatter ships of Tarshish.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 As we have heard, so we have seen, In the city of YHWH of hosts, In the city of our God, God establishes her for all time. (Selah)
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 We have thought, O God, of Your kindness, In the midst of Your temple,
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 As [is] Your Name, O God, so [is] Your praise, Over the ends of the earth, Righteousness has filled Your right hand.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Mount Zion rejoices, The daughters of Judah are joyful, For the sake of Your judgments.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Surround Zion, and go around her, count her towers,
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Set your heart to her bulwark, Consider her high places, So that you recount to a later generation,
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 That this God [is] our God—For all time and forever, He leads us over death!
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.