< Psalms 141 >
1 A PSALM OF DAVID. O YHWH, I have called You, hurry to me, Give ear [to] my voice when I call to You.
Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
2 My prayer is prepared—incense before You, The lifting up of my hands—the evening present.
Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
3 Set, O YHWH, a watch for my mouth, Watch over the door of my lips.
Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
4 Do not incline my heart to an evil thing, To habitually do actions in wickedness, Working iniquity with men, Indeed, I do not eat of their pleasant things.
Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
5 The righteous beat me [in] kindness. And reprove me, My head does not disallow oil of the head, For my prayer [is] still about their distress.
Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
6 Their judges have been released by the sides of a rock, And they have heard my sayings, For they have been pleasant.
Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
7 As one tilling and ripping up in the land, Have our bones been scattered at the command of Saul. (Sheol )
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol )
8 But to You, O YHWH, my Lord, [are] my eyes, In You I have trusted, Do not make my soul bare.
Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
9 Keep me from the trap they laid for me, Even snares of workers of iniquity.
Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 The wicked fall in their dragnets together, until I pass over!
Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.