< Psalms 121 >
1 A SONG OF THE ASCENTS. I lift up my eyes to the hills, From where does my help come?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 My help [is] from YHWH, Maker of the heavens and earth,
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 He does not permit your foot to be moved, He who is preserving you does not slumber.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Behold, He does not slumber, nor sleep, He who is preserving Israel.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 YHWH [is] He who is preserving you, YHWH [is] your shade on your right hand,
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 By day the sun does not strike you, Nor the moon by night.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 YHWH preserves you from all evil, He preserves your soul.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 YHWH preserves your going out and your coming in, From now on—even for all time!
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.