< Psalms 118 >

1 Give thanks to YHWH, For [He is] good, for His kindness [is] for all time.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Now let Israel say, His kindness [is] for all time.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Now let the house of Aaron say, His kindness [is] for all time.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Now let those fearing YHWH say, His kindness [is] for all time.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 I called YAH from the narrow place, YAH answered me in a broad place.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 YHWH [is] for me, I do not fear what man does to me.
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 YHWH [is] for me among my helpers, And I look on those hating me.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Better to take refuge in YHWH, Than to trust in man,
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 Better to take refuge in YHWH, Than to trust in princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 All nations have surrounded me, In the Name of YHWH I surely cut them off.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 They have surrounded me, Indeed, they have surrounded me, In the Name of YHWH I surely cut them off.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 They surrounded me as bees, They have been extinguished as a fire of thorns, In the Name of YHWH I surely cut them off.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 You have severely thrust me to fall, And YHWH has helped me.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 YAH is my strength and song, And He is to me for salvation.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 A voice of singing and salvation, [Is] in the tents of the righteous, The right hand of YHWH is doing valiantly.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 The right hand of YHWH is exalted, The right hand of YHWH is doing valiantly.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 I do not die, but live, And recount the works of YAH,
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 YAH has severely disciplined me, And has not given me up to death.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Open gates of righteousness to me, I enter into them—I thank YAH.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 This [is] the gate to YHWH, The righteous enter into it.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 I thank You, for You have answered me, And are to me for salvation.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 A stone the builders refused Has become head of a corner.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 This has been from YHWH, It [is] wonderful in our eyes,
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 This [is] the day YHWH has made, We rejoice and are glad in it.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Ah, now, O YHWH, please save, Ah, now, O YHWH, please prosper.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Blessed [is] He who is coming In the Name of YHWH, We blessed you from the house of YHWH,
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 God [is] YHWH, and He gives light to us, Direct the festal-sacrifice with cords, To the horns of the altar.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 You [are] my God, and I confess You, My God, I exalt You.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Give thanks to YHWH, For [He is] good, for His kindness [is] for all time!
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psalms 118 >