< Psalms 116 >

1 I have loved, because YHWH hears My voice, my supplication,
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Because He has inclined His ear to me, And during my days I call.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Cords of death have surrounded me, And straits of Sheol have found me, I find distress and sorrow. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 And in the Name of YHWH I call: Ah, now, O YHWH, deliver my soul,
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 YHWH [is] gracious, and righteous, Indeed, our God [is] merciful,
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 YHWH [is] a preserver of the simple, I was low, and He gives salvation to me.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Return, O my soul, to your rest, For YHWH has conferred benefits on you.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 For You have delivered my soul from death, My eyes from tears, my feet from overthrowing.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 I habitually walk before YHWH In the lands of the living.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 I have believed, for I speak, I have been greatly afflicted.
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 I said in my haste, “Every man [is] a liar.”
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 What do I return to YHWH? All His benefits [are] on me.
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 I lift up the cup of salvation, And in the Name of YHWH I call.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Let me complete my vows to YHWH, Now, before all His people.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Precious in the eyes of YHWH [is] the death of His saints.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Ah, now, O YHWH, for I [am] Your servant; I [am] Your servant, son of Your handmaid; You have opened my bonds.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 I sacrifice a sacrifice of thanks to You, And in the Name of YHWH I call.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Let me complete my vows to YHWH, Now, before all His people,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 In the courts of the house of YHWH, In your midst, O Jerusalem, praise YAH!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 116 >