< Proverbs 4 >

1 Hear, you sons, the instruction of a father, And give attention to know understanding.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 For I have given to you good learning, do not forsake my law.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 For I have been a son to my father—tender, And an only one before my mother.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 And he directs me, and he says to me: “Let your heart retain my words, Keep my commands, and live.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Get wisdom, get understanding, Do not forget, nor turn away From the sayings of my mouth.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Do not forsake her, and she preserves you, Love her, and she keeps you.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 The first thing [is] wisdom—get wisdom, And with all your getting get understanding.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Exalt her and she lifts you up, She honors you when you embrace her.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 She gives a wreath of grace to your head, She gives you a crown of beauty freely.”
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Hear, my son, and receive my sayings, And years of life [are] multiplied to you.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 I have directed you in a way of wisdom, I have caused you to tread in paths of uprightness.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 In your walking your step is not restricted, And if you run, you do not stumble.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Lay hold on instruction, do not desist, Keep her, for she [is] your life.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Do not enter into the path of the wicked, And do not be blessed in a way of evildoers.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Avoid it, do not pass over into it, Turn aside from it, and pass on.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 For they do not sleep if they do no evil, And their sleep has been taken away violently, If they do not cause [some] to stumble.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 For they have eaten bread of wickedness, And they drink wine of violence.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 And the path of the righteous [is] as a shining light, Going and brightening until the day is established,
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 The way of the wicked [is] as darkness, They have not known at what they stumble.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 My son, give attention to my words, Incline your ear to my sayings,
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Do not let them turn aside from your eyes, Preserve them in the midst of your heart.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 For they [are] life to those finding them, And healing to all their flesh.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Above every charge keep your heart, For out of it [are] the outgoings of life.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Turn aside a contrary mouth from you, And put perverse lips far from you,
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Your eyes look straightforward, And your eyelids look straight before you.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Ponder the path of your feet, And all your ways [are] established.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Do not incline [to] the right or to the left, Turn aside your foot from evil!
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Proverbs 4 >