< Proverbs 3 >
1 My son! Do not forget my law, And let your heart keep my commands,
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 For [the] length of [your] days and years, Life and peace they add to you.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Do not let kindness and truth forsake you, Bind them on your neck, Write them on the tablet of your heart,
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 And find grace and good understanding In the eyes of God and man.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Trust to YHWH with all your heart, And do not lean to your own understanding.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 In all your ways know Him, And He makes your paths straight.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Do not be wise in your own eyes, Fear YHWH, and turn aside from evil.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 It is healing to your navel, And moistening to your bones.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honor YHWH from your substance, And from the beginning of all your increase;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 And your barns are filled [with] plenty, And your presses break forth [with] new wine.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Discipline of YHWH, my son, do not despise, And do not be distressed with His reproof,
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 For whom YHWH loves He reproves, Even as a father the son He is pleased with.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 O the blessedness of a man [who] has found wisdom, And of a man [who] brings forth understanding.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 For better [is] her merchandise Than the merchandise of silver, And than gold—her increase.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 She [is] precious above rubies, And all your pleasures are not comparable to her.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Length of days [is] in her right hand, In her left [are] wealth and honor.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Her ways [are] ways of pleasantness, And all her paths [are] peace.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 She [is] a tree of life to those laying hold on her, And whoever is retaining her [is] blessed.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 YHWH founded the earth by wisdom, He prepared the heavens by understanding.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 By His knowledge depths have been broken, And clouds drop dew.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 My son! Do not let them turn from your eyes, Keep wisdom and thoughtfulness,
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 And they are life to your soul, and grace to your neck.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Then you go your way confidently, And your foot does not stumble.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 If you lie down, you are not afraid, Indeed, you have lain down, And your sleep has been sweet.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Do not be afraid of sudden fear, And of the desolation of the wicked when it comes.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 For YHWH is at your side, And He has kept your foot from capture.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Do not withhold good from its owners, When your hand [is] toward God to do [it].
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Do not say to your friend, “Go, and return, and tomorrow I give,” When substance [is] with you.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Do not devise evil against your neighbor, And he sitting confidently with you.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Do not strive with a man without cause, If he has not done you evil.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Do not be envious of a man of violence, Nor fix on any of his ways.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 For the perverted [is] an abomination to YHWH, And His secret counsel [is] with the upright.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 The curse of YHWH [is] in the house of the wicked. And He blesses the habitation of the righteous.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 If He scorns the scorners, Yet He gives grace to the humble.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 The wise inherit glory, And fools are bearing away shame!
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.