< Proverbs 23 >

1 When you sit to eat with a ruler, Diligently consider that which [is] before you,
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 And you have put a knife to your throat, If you [are] a man of appetite.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Have no desire to his delicacies, seeing it [is] lying food.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Do not labor to make wealth, Cease from your own understanding, Do you cause your eyes to fly on it? Then it is not.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 For wealth makes wings to itself, It flies to the heavens as an eagle.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Do not eat the bread of an evil eye, And have no desire to his delicacies,
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 For as he has thought in his soul, so he [is]. “Eat and drink,” he says to you, And his heart [is] not with you.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 You vomit up your morsel you have eaten, And have marred your words that [are] sweet.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Do not speak in the ears of a fool, For he treads on the wisdom of your words.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Do not remove a border of ancient times, And do not enter into fields of the fatherless,
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 For their Redeemer [is] strong, He pleads their cause with you.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Bring your heart to instruction, And your ear to sayings of knowledge.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Do not withhold discipline from a youth, When you strike him with a rod he does not die.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 You strike him with a rod, And you deliver his soul from Sheol. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 My son, if your heart has been wise, My heart rejoices, even mine,
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 And my reins exult when your lips speak uprightly.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Do not let your heart be envious at sinners, But—in the fear of YHWH all the day.
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 For is there a posterity? Then your hope is not cut off.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Hear, my son, and be wise, And make your heart blessed in the way,
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Do not become drunk with wine, Among gluttonous ones of flesh,
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 For the drunkard and glutton become poor, And drowsiness clothes with rags.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Listen to your father, who begot you, And do not despise your mother when she has become old.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Buy truth, and do not sell, Wisdom, and instruction, and understanding,
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 The father of the righteous rejoices greatly, The begetter of the wise rejoices in him.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Your father and your mother rejoice, Indeed, she bearing you is joyful.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Give, my son, your heart to me, And let your eyes watch my ways.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 For a harlot [is] a deep ditch, And a strange woman [is] a narrow pit.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 She also, as catching prey, lies in wait, And she increases the treacherous among men.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Who has woe? Who has sorrow? Who has contentions? Who has complaint? Who has wounds without cause? Who has redness of eyes?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Those lingering by the wine, Those going in to search out mixed wine.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Do not see wine when it shows itself red, When it gives its color in the cup, It goes up and down through the upright.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 Its latter end—it bites as a serpent, And it stings as a viper.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Your eyes see strange women, And your heart speaks perverse things.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 And you have been as one lying down in the heart of the sea, And as one lying down on the top of a mast.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 “They struck me, I have not been sick, They beat me, I have not known. When I awake—I seek it yet again!”
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Proverbs 23 >