< Proverbs 2 >
1 My son, if you accept my sayings, And lay up my commands with you,
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 To cause your ear to attend to wisdom, You incline your heart to understanding,
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 For if you call for intelligence, [And] give forth your voice for intelligence,
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 If you seek her as silver, And search for her as hid treasures,
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 Then you understand the fear of YHWH, And you find the knowledge of God.
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 For YHWH gives wisdom, Knowledge and understanding from His mouth.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Even to lay up substance for the upright, A shield for those walking uprightly.
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 To keep the paths of judgment, And He preserves the way of His saints.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Then you understand righteousness, And judgment, and uprightness—every good path.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 For wisdom comes into your heart, And knowledge is pleasant to your soul,
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Thoughtfulness watches over you, Understanding keeps you,
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 To deliver you from an evil way, From any speaking contrary things,
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 Who are forsaking paths of uprightness, To walk in ways of darkness,
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Who are rejoicing to do evil, They delight in [the] contrariness of the wicked,
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Whose paths [are] crooked, Indeed, they are perverted in their ways.
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 To deliver you from the strange woman, From the stranger who has made her sayings smooth,
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 Who is forsaking the guide of her youth, And has forgotten the covenant of her God.
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 For her house has inclined to death, And her paths to Rephaim.
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 None going in to her return, Nor do they reach the paths of life.
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 That you go in the way of the good, And keep the paths of the righteous.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 For the upright inhabit the earth, And the perfect are left in it,
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 And the wicked are cut off from the earth, And treacherous dealers plucked out of it!
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.